< 1 Samuel 28 >

1 And it came to pass in those days, that the Philistines gathered together their armies to be prepared for war against Israel: and Achis said to David: Know thou now assuredly, that thou shalt go out with me to the war, thou, and thy men.
Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
2 And David said to Achis: Now thou shalt know what thy servant will do. And Achis said to David: And I will appoint thee to guard my life for ever.
Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
3 Now Samuel was dead, and all Israel mourned for him, and buried him in Ramatha his city. And Saul had put away all the magicians and soothsayers out of the land.
Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
4 And the Philistines were gathered together, and came and camped in Sunam: and Saul also gathered together all Israel, and came to Gelboe.
Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
5 And Saul saw the army of the Plilistines, and was afraid, and his heart was very much dismayed.
Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
6 And he consulted the Lord, and he answered him not, neither by dreams, nor by priests, nor by prophets.
Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
7 And Saul said to his servants: Seek me a woman that hath a divining spirit, and I will go to her, and inquire by her. And his servants said to him: There is a woman that hath a divining spirit at Endor.
Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
8 Then he disguised himself: and put on other clothes, and he went, and two men with him, and they came to the woman by night, and he said to her: Divine to me by thy divining spirit, and bring me up him whom I shall tell thee.
Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
9 And the woman said to him: Behold thou knowest all that Saul hath done, and how he hath rooted out the magicians and soothsayers from the land: why then dost thou lay a snare for my life, to cause me to be put to death?
Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
10 And Saul swore unto her by the Lord, saying: As the Lord liveth there shall no evil happen to thee for this thing.
Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
11 And the woman said to him: Whom shall I bring up to thee? And he said, Bring me up Samuel.
Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
12 And when the woman saw Samuel, she cried out with a loud voice, and said to Saul: Why hast thou deceived me? for thou art Saul.
Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
13 And the king said to her: Fear not: what hast thou seen? And the woman said to Saul: I saw gods ascending out of the earth.
Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
14 And he said to her: What form is he of? And she said: An old man cometh up, and he is covered with a mantle. And Saul understood that it was Samuel, and he bowed himself with his face to the ground, and adored.
Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
15 And Samuel said to Saul: Why hast thou disturbed my rest, that I should be brought up? And Saul said, I am in great distress: for the Philistines fight against me, and God is departed from me, and would not hear me, neither by the hand of prophets, nor by dreams: therefore I have called thee, that thou mayest shew me what I shall do.
Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
16 And Samuel said: Why askest thou me, seeing the Lord has departed from thee, and is gone over to thy rival:
Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
17 For the Lord will do to thee as he spoke by me, and he will rend thy kingdom out of thy hand, and will give it to thy neighbour David:
Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
18 Because thou didst not obey the voice of the Lord, neither didst thou execute the wrath of his indignation upon Amalec. Therefore hath the Lord done to thee what thou sufferest this day.
Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
19 And the Lord also will deliver Israel with thee into the hands of the Philistines: and tomorrow thou and thy sons shall be with me: and the Lord will also deliver the army of Israel into the hands of the Philistines.
Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
20 And forthwith Saul fell all along on the ground, for he was frightened with the words of Samuel, and there was no strength in him, for he had eaten no bread all that day.
Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
21 And the woman came to Saul (for he was very much troubled) and said to him: Behold thy handmaid hath obeyed thy voice, and I have put my life in my hand: and I hearkened unto the words which thou spokest to me.
Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
22 Now therefore hear thou also the voice of thy handmaid, and let me set before thee a morsel of bread, that thou mayest eat and recover strength, and be able to go on thy journey.
Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
23 But he refused, and said: I will not eat. But his servants and the woman forced him, and at length hearkening to their voice, he arose from the ground and sat upon the bed.
Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
24 Now the woman had a fatted calf in the house, and she made haste and killed it: and taking meal kneaded it, and baked some unleavened bread,
Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
25 And set it before Saul, and before his servants. And when they had eaten they rose up, and walked all that night.
Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.

< 1 Samuel 28 >