< 1 Samuel 20 >
1 But David fled from Najoth, which is in Ramatha, and came and said to Jonathan: What have I done? what is my iniquity, and what is my sin against thy father, that he seeketh my life?
Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
2 And he said to him: God forbid, thou shalt not die: for my father will do nothing great or little, without first telling me: hath then my father hid this word only from me? no, this shall not be.
Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
3 And he swore again to David. And David said: Thy father certainly knoweth that I have found grace in thy sight, and he will say: Let not Jonathan know this, lest he be grieved. But truly as the Lord liveth, and thy soul liveth, there is but one step (as I may say) between me and death.
Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
4 And Jonathan said to David: Whatsoever thy soul shall say to me, I will do for thee.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
5 And David said to Jonathan: Behold tomorrow is the new moon, and I according to custom am wont to sit beside the king to eat: let me go then that I may be hid in the field till the evening of the third day.
Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
6 If thy father look and inquire for me, thou shalt answer him: David asked me that he might run to Bethlehem his own city: because there are solemn sacrifices there for all his tribe.
Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
7 If he shall say, It is well: thy servant shall have peace: but if he be angry, know that his malice is come to its height.
Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
8 Deal mercifully then with thy servant: for thou hast brought me thy servant into a covenant of the Lord with thee. But if there be any iniquity in me, do thou kill me, and bring me not in to thy father.
Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
9 And Jonathan said: Far be this from thee: for if I should certainly know that evil is determined by my father against thee, I could do no otherwise than tell thee.
Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
10 And David answered Jonathan: Who shall bring me word, if thy father should answer thee harshly concerning me?
Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
11 And Jonathan said to David: Come and let us go out into the field. And when they were both of them gone out into the field,
Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
12 Jonathan said to David: O Lord God of Israel, if I shall discover my father’s mind, tomorrow or the day after, and there be any thing good for David, and I send not immediately to thee, and make it known to thee,
Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
13 May the Lord do so and so to Jonathan and add still more. But if my father shall continue in malice against thee, I will discover it to thy ear, and will send thee away, that thou mayest go in peace, and the Lord be with thee, as he hath been with my father.
Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
14 And if I live, thou shalt shew me the kindness of the Lord: but if I die,
Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
15 Thou shalt not take away thy kindness from my house for ever, when the Lord shall have rooted out the enemies of David, every one of them from the earth, may he take away Jonathan from his house, and may the Lord require it at the hands of David’s enemies.
Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
16 Jonathan therefore made a covenant with the house of David: and the Lord required it at the hands of David’s enemies.
“Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
17 And Jonathan swore again to David, because he loved him: for he loved him as his own soul.
Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
18 And Jonathan said to him: Tomorrow is the new moon, and thou wilt be missed:
Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
19 For thy seat will be empty till after tomorrow. So thou shalt go down quickly, and come to the place, where thou must be hid on the day when it is lawful to work, and thou shalt remain beside the stone, which is called Ezel.
Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
20 And I will shoot three arrows near it, and will shoot as if I were exercising myself at a mark.
Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
21 And I will send a boy, saying to him: Go and fetch me the arrows.
Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
22 If I shall say to the boy: Behold the arrows are on this side of thee, take them up: come thou to me, because, there is peace to thee, and there is no evil, as the Lord liveth. But if I shall speak thus to the boy: Behold the arrows are beyond thee: go in peace, for the Lord hath sent thee away.
Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
23 And concerning the word which I and thou have spoken, the Lord be between thee and me for ever.
Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
24 So David was hid in the field, and the new moon came, and the king sat down to eat bread.
Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
25 And when the king sat down upon his chair (according to custom) which was beside the wall, Jonathan arose, and Abner sat by Saul’s side, and David’s place appeared empty.
Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
26 And Saul said nothing that day, for he thought it might have happened to him, that he was not clean, nor purified.
Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
27 And when the second day after the new moon was come, David’s place appeared empty again. And Saul said to Jonathan his son: Why cometh not the son of Isai to meat neither yesterday nor today?
Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
28 And Jonathan answered Saul: He asked leave of me earnestly to go to Bethlehem,
Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
29 And he said: Let me go, for there is a solemn sacrifice in the city, one of my brethren hath sent for me: and now if I have found favour in thy eyes, I will go quickly, and see my brethren. For this cause he came not to the king’s table.
Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
30 Then Saul being angry against Jonathan said to him: Thou son of a woman that is the ravisher of a man, do I not know that thou lovest the son of Isai to thy own confusion and to the confusion of thy shameless mother?
Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
31 For as long as the son of Isai liveth upon earth, thou shalt not be established, nor thy kingdom. Therefore now presently send, and fetch him to me: for he is the son of death.
Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
32 And Jonathan answering Saul his father, said: Why shall he die: what hath he done?
Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
33 And Saul caught up a spear to strike him. And Jonathan understood that it was determined by his father to kill David.
Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
34 So Jonathan rose from the table in great anger, and did not eat bread on the second day after the new moon. For he was grieved for David, because his father had put him to confusion.
Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
35 And when the morning came, Jonathan went into the field, according to the appointment with David, and a little boy with him.
Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
36 And he said to his boy: Go, and fetch me the arrows which I shoot. And when the boy ran, he shot another arrow beyond the boy.
Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
37 The boy therefore came to the place of the arrow which Jonathan had shot: and Jonathan cried after the boy, and said: Behold the arrow is there further beyond thee.
Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
38 And Jonathan cried again after the boy, saying: Make haste speedily, stand not. And Jonathan’s boy gathered up the arrows, and brought them to his master:
Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
39 And he knew not at all what was doing: for only Jonathan and David knew the matter.
(Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
40 Jonathan therefore gave his arms to the boy, and said to him: Go, and carry them into the city.
Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
41 And when the boy was gone, David rose out of his place, which was towards the south, and falling on his face to the ground, adored thrice: and kissing one another, they wept together, but David more.
Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
42 And Jonathan said to David: Go in peace: and let all stand that we have sworn both of us in the name of the Lord, saying: The Lord be between me and thee, and between my seed and thy seed for ever. And David arose, and departed: and Jonathan went into the city.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.