< Titus 3 >
1 Put them in mind to be subject to rulers, to authorities, to be obedient to rule, to be ready to do every good work,
Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
2 to speak evil of no one, not to be contentious, [to be] mild, shewing all meekness towards all men.
Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
3 For we were once ourselves also without intelligence, disobedient, wandering in error, serving various lusts and pleasures, living in malice and envy, hateful, [and] hating one another.
Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
4 But when the kindness and love to man of our Saviour God appeared,
Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
5 not on the principle of works which [have been done] in righteousness which we had done, but according to his own mercy he saved us through [the] washing of regeneration and renewal of [the] Holy Spirit,
Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
6 which he poured out on us richly through Jesus Christ our Saviour;
amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
7 that, having been justified by his grace, we should become heirs according to [the] hope of eternal life. (aiōnios )
kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios )
8 The word [is] faithful, and I desire that thou insist strenuously on these things, that they who have believed God may take care to pay diligent attention to good works. These things are good and profitable to men.
Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
9 But foolish questions, and genealogies, and strifes, and contentions about the law, shun; for they are unprofitable and vain.
Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
10 An heretical man after a first and second admonition have done with,
Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
11 knowing that such a one is perverted, and sins, being self-condemned.
Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
12 When I shall send Artemas to thee, or Tychicus, use diligence to come to me to Nicopolis; for I have decided to winter there.
Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
13 Zenas the lawyer and Apollos set forward diligently on their way, that nothing may be lacking to them;
Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
14 and let ours also learn to apply themselves to good works for necessary wants, that they may not be unfruitful.
Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
15 All with me salute thee. Salute those who love us in [the] faith. Grace [be] with you all.
Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.