< Revelation 9 >
1 And the fifth angel sounded [his] trumpet: and I saw a star out of the heaven fallen to the earth; and there was given to it the key of the pit of the abyss. (Abyssos )
Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos )
2 And it opened the pit of the abyss; and there went up smoke out of the pit as [the] smoke of a great furnace; and the sun and the air were darkened with the smoke of the pit. (Abyssos )
Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos )
3 And out of the smoke came forth locusts on the earth, and power was given to them as the scorpions of the earth have power;
Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi.
4 and it was said to them, that they should not injure the grass of the earth, nor any green thing, nor any tree, but the men who have not the seal of God on their foreheads:
Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo.
5 and it was given to them that they should not kill them, but that they should be tormented five months; and their torment [was] as [the] torment of a scorpion when it strikes a man.
Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu.
6 And in those days shall men seek death, and shall in no way find it; and shall desire to die, and death flees from them.
Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.
7 And the likenesses of the locusts [were] like to horses prepared for war; and upon their heads as crowns like gold, and their faces as faces of men;
Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu.
8 and they had hair as women's hair, and their teeth were as of lions,
Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango.
9 and they had breastplates as breastplates of iron, and the sound of their wings [was] as the sound of chariots of many horses running to war;
Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo.
10 and they have tails like scorpions, and stings; and their power [was] in their tails to hurt men five months.
Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu.
11 They have a king over them, the angel of the abyss: his name in Hebrew, Abaddon, and in Greek he has [for] name Apollyon. (Abyssos )
Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos )
12 The first woe has passed. Behold, there come yet two woes after these things.
Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.
13 And the sixth angel sounded [his] trumpet: and I heard a voice from the four horns of the golden altar which [is] before God,
Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu.
14 saying to the sixth angel that had the trumpet, Loose the four angels which are bound at the great river Euphrates.
Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.”
15 And the four angels were loosed, who are prepared for the hour and day and month and year, that they might slay the third part of men;
Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu.
16 and the number of the hosts of horse [was] twice ten thousand times ten thousand. I heard their number.
Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.
17 And thus I saw the horses in the vision, and those that sat upon them, having breastplates of fire and jacinth and brimstone; and the heads of the horses [were] as heads of lions, and out of their mouths goes out fire and smoke and brimstone.
Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule.
18 By these three plagues were the third part of men killed, by the fire and the smoke and the brimstone which goes out of their mouths.
Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo.
19 For the power of the horses is in their mouth and in their tails: for their tails [are] like serpents, having heads, and with them they injure.
Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.
20 And the rest of men who were not killed with these plagues repented not of the works of their hands, that they should not worship demons, and the golden and silver and brazen and stone and wooden idols, which can neither see nor hear nor walk.
Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula.
21 And they repented not of their murders, nor of their witchcrafts, nor of their fornication, nor of their thefts.
Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.