< Psalms 97 >
1 Jehovah reigneth: let the earth be glad, let the many isles rejoice.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Clouds and darkness are round about him; righteousness and judgment are the foundation of his throne.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 A fire goeth before him, and burneth up his adversaries round about.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 His lightnings lightened the world: the earth saw, and trembled.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 The mountains melted like wax at the presence of Jehovah, at the presence of the Lord of the whole earth.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 The heavens declare his righteousness, and all the peoples see his glory.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Ashamed be all they that serve graven images, that boast themselves of idols. Worship him, all ye gods.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Zion heard, and rejoiced; and the daughters of Judah were glad, because of thy judgments, O Jehovah.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 For thou, Jehovah, art the Most High above all the earth; thou art exalted exceedingly above all gods.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Ye that love Jehovah, hate evil: he preserveth the souls of his saints, he delivereth them out of the hand of the wicked.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Light is sown for the righteous, and joy for the upright in heart.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Rejoice in Jehovah, ye righteous; and give thanks in remembrance of his holiness.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.