< Psalms 92 >

1 A Psalm, a Song, for the Sabbath day. It is good to give thanks unto Jehovah, and to sing psalms unto thy name, O Most High;
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 To declare thy loving-kindness in the morning, and thy faithfulness in the nights,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 Upon an instrument of ten strings and upon the lute; upon the Higgaion with the harp.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 For thou, Jehovah, hast made me glad through thy work; I will triumph in the works of thy hands.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Jehovah, how great are thy works! Thy thoughts are very deep:
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 A brutish man knoweth not, neither doth a fool understand it.
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 When the wicked spring as the grass, and when all the workers of iniquity flourish, it is that they may be destroyed for ever.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 And thou, Jehovah, art on high for evermore.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 For lo, thine enemies, O Jehovah, for lo, thine enemies shall perish; all the workers of iniquity shall be scattered.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 But my horn shalt thou exalt like a buffalo's: I shall be anointed with fresh oil.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 And mine eye shall see [its desire] on mine enemies; mine ears shall hear [it] of the evil-doers that rise up against me.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 The righteous shall shoot forth like a palm-tree; he shall grow like a cedar on Lebanon.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 Those that are planted in the house of Jehovah shall flourish in the courts of our God:
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 They are still vigorous in old age, they are full of sap and green;
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 To shew that Jehovah is upright: [he is] my rock, and there is no unrighteousness in him.
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Psalms 92 >