< Psalms 9 >
1 To the chief Musician. Upon Muthlabben. A Psalm of David. I will praise Jehovah with my whole heart; I will recount all thy marvellous works.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 I will be glad and rejoice in thee; I will sing forth thy name, O Most High.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 When mine enemies turned back, they stumbled and perished at thy presence:
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 For thou hast maintained my right and my cause. Thou sittest on the throne, judging righteously.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Thou hast rebuked the nations, thou hast destroyed the wicked; thou hast put out their name for ever and ever.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 O enemy! destructions are ended for ever. — Thou hast also destroyed cities, even the remembrance of them hath perished.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 But Jehovah sitteth for ever; he hath ordained his throne for judgment.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 And it is he that will judge the world with righteousness; he shall execute judgment upon the peoples with equity.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 And Jehovah will be a refuge to the oppressed one, a refuge in times of distress.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 And they that know thy name will confide in thee; for thou, Jehovah, hast not forsaken them that seek thee.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Sing psalms to Jehovah who dwelleth in Zion; tell among the peoples his doings.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 For when he maketh inquisition for blood, he remembereth them; the cry of the afflicted ones hath he not forgotten.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Be gracious unto me, O Jehovah; consider mine affliction from them that hate me, lifting me up from the gates of death:
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 That I may declare all thy praise in the gates of the daughter of Zion. I will be joyful in thy salvation.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 The nations are sunk down in the pit [that] they made; in the net that they hid is their own foot taken.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Jehovah is known [by] the judgment he hath executed: the wicked is ensnared in the work of his own hands. (Higgaion, Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 The wicked shall be turned into Sheol, all the nations that forget God. (Sheol )
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol )
18 For the needy one shall not be forgotten alway; the hope of the meek shall not perish for ever.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Arise, Jehovah; let not man prevail: let the nations be judged in thy sight.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Put them in fear, Jehovah: that the nations may know themselves to be but men. (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)