< Psalms 29 >

1 A Psalm of David. Give unto Jehovah, ye sons of the mighty ones, give unto Jehovah glory and strength;
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Give unto Jehovah the glory of his name; worship Jehovah in holy splendour.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 The voice of Jehovah is upon the waters: the God of glory thundereth, — Jehovah upon great waters.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 The voice of Jehovah is powerful; the voice of Jehovah is full of majesty.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 The voice of Jehovah breaketh cedars; yea, Jehovah breaketh the cedars of Lebanon:
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 And he maketh them to skip like a calf, Lebanon and Sirion like a young buffalo.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 The voice of Jehovah cleaveth out flames of fire.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 The voice of Jehovah shaketh the wilderness; Jehovah shaketh the wilderness of Kadesh.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 The voice of Jehovah maketh the hinds to calve, and layeth bare the forests; and in his temple doth every one say, Glory!
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Jehovah sitteth upon the flood; yea, Jehovah sitteth as king for ever.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Jehovah will give strength unto his people; Jehovah will bless his people with peace.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psalms 29 >