< Psalms 24 >

1 Of David. A Psalm. The earth is Jehovah's, and the fulness thereof; the world, and they that dwell therein.
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 For it was he that founded it upon seas, and established it upon floods.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Who shall ascend into the mount of Jehovah? and who shall stand in his holy place?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 He that hath blameless hands and a pure heart; who lifteth not up his soul unto vanity, nor sweareth deceitfully:
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 He shall receive blessing from Jehovah, and righteousness from the God of his salvation.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 This is the generation of them that seek unto him, that seek thy face, O Jacob. (Selah)
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Lift up your heads, ye gates, and be ye lifted up, ye everlasting doors, and the King of glory shall come in.
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Who is this King of glory? Jehovah strong and mighty, Jehovah mighty in battle.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Lift up your heads, ye gates; yea, lift up, ye everlasting doors, and the King of glory shall come in.
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Who is he, this King of glory? Jehovah of hosts, he is the King of glory. (Selah)
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)

< Psalms 24 >