< Psalms 2 >

1 Why are the nations in tumultuous agitation, and [why] do the peoples meditate a vain thing?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 The kings of the earth set themselves, and the princes plot together, against Jehovah and against his anointed:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Let us break their bonds asunder, and cast away their cords from us!
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 He that dwelleth in the heavens shall laugh, the Lord shall have them in derision.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Then will he speak to them in his anger, and in his fierce displeasure will he terrify them:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 And I have anointed my king upon Zion, the hill of my holiness.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 I will declare the decree: Jehovah hath said unto me, Thou art my Son; I this day have begotten thee.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Ask of me, and I will give thee nations for an inheritance, and for thy possession the ends of the earth:
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Thou shalt break them with a sceptre of iron, as a potter's vessel thou shalt dash them in pieces.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 And now, O kings, be ye wise, be admonished, ye judges of the earth.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serve Jehovah with fear, and rejoice with trembling.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Kiss the Son, lest he be angry, and ye perish in the way, though his anger burn but a little. Blessed are all who have their trust in him.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalms 2 >