< Psalms 150 >
1 Hallelujah! Praise God in his sanctuary; praise him in the firmament of his power.
Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Praise him in his mighty acts; praise him according to the abundance of his greatness.
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Praise him with the sound of the trumpet; praise him with lute and harp;
Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Praise him with the tambour and dance; praise him with stringed instruments and the pipe;
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Praise him with loud cymbals; praise him with high sounding cymbals.
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 Let everything that hath breath praise Jah. Hallelujah!
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.