< Psalms 122 >
1 A Song of degrees. Of David. I rejoiced when they said unto me, Let us go into the house of Jehovah.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Our feet shall stand within thy gates, O Jerusalem.
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jerusalem, which art built as a city that is compact together,
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 Whither the tribes go up, the tribes of Jah, a testimony to Israel, to give thanks unto the name of Jehovah.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 For there are set thrones for judgment, the thrones of the house of David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Pray for the peace of Jerusalem: they shall prosper that love thee.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Peace be within thy bulwarks, prosperity within thy palaces.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 For my brethren and companions' sakes I will say, Peace be within thee!
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 Because of the house of Jehovah our God I will seek thy good.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.