< Psalms 121 >
1 A Song of degrees. I lift up mine eyes unto the mountains: whence shall my help come?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 My help [cometh] from Jehovah, who made the heavens and the earth.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 He will not suffer thy foot to be moved; he that keepeth thee will not slumber.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Behold, he that keepeth Israel will neither slumber nor sleep.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Jehovah is thy keeper, Jehovah is thy shade upon thy right hand;
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 The sun shall not smite thee by day, nor the moon by night.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Jehovah will keep thee from all evil; he will keep thy soul.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Jehovah will keep thy going out and thy coming in, from henceforth and for evermore.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.