< Psalms 118 >
1 Give ye thanks unto Jehovah; for he is good; for his loving-kindness [endureth] for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Oh let Israel say, that his loving-kindness [endureth] for ever.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Oh let the house of Aaron say, that his loving-kindness [endureth] for ever.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Oh let them that fear Jehovah say, that his loving-kindness [endureth] for ever.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 I called upon Jah in distress; Jah answered me [and set me] in a large place.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Jehovah is for me, I will not fear; what can man do unto me?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Jehovah is for me among them that help me; and I shall see [my desire] upon them that hate me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is better to trust in Jehovah than to put confidence in man;
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is better to trust in Jehovah than to put confidence in nobles.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations encompassed me; but in the name of Jehovah have I destroyed them.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They encompassed me, yea, encompassed me; but in the name of Jehovah have I destroyed them.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They encompassed me like bees; they are quenched as the fire of thorns: for in the name of Jehovah have I destroyed them.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Thou hast thrust hard at me that I might fall; but Jehovah helped me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 My strength and song is Jah, and he is become my salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The voice of triumph and salvation is in the tents of the righteous: the right hand of Jehovah doeth valiantly;
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of Jehovah is exalted, the right hand of Jehovah doeth valiantly.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I shall not die, but live, and declare the works of Jah.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Jah hath chastened me sore; but he hath not given me over unto death.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open to me the gates of righteousness: I will enter into them; Jah will I praise.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This is the gate of Jehovah: the righteous shall enter therein.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I will give thee thanks, for thou hast answered me, and art become my salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 [The] stone which the builders rejected hath become the head of the corner:
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This is of Jehovah; it is wonderful in our eyes.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the day that Jehovah hath made; we will rejoice and be glad in it.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Oh save, Jehovah, I beseech thee; Jehovah, I beseech thee, oh send prosperity!
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed be he that cometh in the name of Jehovah. We have blessed you out of the house of Jehovah.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Jehovah is God, and he hath given us light: bind the sacrifice with cords, — up to the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Thou art my God, and I will give thee thanks; my God, I will exalt thee.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Give ye thanks unto Jehovah; for he is good; for his loving-kindness [endureth] for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.