< Psalms 115 >
1 Not unto us, O Jehovah, not unto us, but unto thy name give glory, for thy loving-kindness and for thy truth's sake.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Wherefore should the nations say, Where then is their God?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 But our God is in the heavens: he hath done whatsoever he pleased.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Their idols are silver and gold, the work of men's hands:
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 They have a mouth, and they speak not; eyes have they, and they see not;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 They have ears, and they hear not; a nose have they, and they smell not;
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 They have hands, and they handle not; feet have they, and they walk not; they give no sound through their throat.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 They that make them are like unto them, — every one that confideth in them.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 O Israel, confide thou in Jehovah: he is their help and their shield.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 House of Aaron, confide in Jehovah: he is their help and their shield.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Ye that fear Jehovah, confide in Jehovah: he is their help and their shield.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Jehovah hath been mindful of us: he will bless, he will bless the house of Israel; he will bless the house of Aaron;
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 He will bless them that fear Jehovah, both the small and the great.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Jehovah will add unto you more, unto you and unto your children.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Ye are blessed of Jehovah, who made the heavens and the earth.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 The heavens are the heavens of Jehovah, but the earth hath he given to the children of men.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 The dead praise not Jah, neither any that go down into silence;
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 But we will bless Jah from this time forth and for evermore. Hallelujah!
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.