< Psalms 112 >
1 Hallelujah! Blessed is the man that feareth Jehovah, that delighteth greatly in his commandments.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 His seed shall be mighty in the land; the generation of the upright shall be blessed.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Wealth and riches [shall be] in his house; and his righteousness abideth for ever.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Unto the upright there ariseth light in the darkness; he is gracious, and merciful, and righteous.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 It is well with the man that is gracious and lendeth; he will sustain his cause in judgment.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 For he shall not be moved for ever: the righteous shall be in everlasting remembrance.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 He shall not be afraid of evil tidings; his heart is fixed confiding in Jehovah;
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 His heart is maintained, he is not afraid, until he see [his desire] upon his oppressors.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 He scattereth abroad, he giveth to the needy; his righteousness abideth for ever: his horn shall be exalted with honour.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 The wicked [man] shall see [it] and be vexed; he shall gnash with his teeth, and melt away: the desire of the wicked shall perish.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.