< Proverbs 9 >
1 Wisdom hath built her house, she hath hewn out her seven pillars;
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 she hath slaughtered her cattle, she hath mingled her wine, she hath also prepared her table;
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 she hath sent forth her maidens: she crieth upon the summits of the high places of the city,
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Whoso is simple, let him turn in hither. To him that is void of understanding, she saith,
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Come, eat ye of my bread, and drink of the wine that I have mingled.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Forsake follies and live, and go in the way of intelligence.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 He that instructeth a scorner getteth to himself shame; and he that reproveth a wicked [man] [getteth] to himself a blot.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Reprove not a scorner, lest he hate thee; reprove a wise [man], and he will love thee.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Impart to a wise [man], and he will become yet wiser; teach a righteous [man], and he will increase learning.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 The fear of Jehovah is the beginning of wisdom; and the knowledge of the Holy is intelligence.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 For by me thy days shall be multiplied, and years of life shall be added to thee.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 If thou art wise, thou shalt be wise for thyself; and if thou scornest, thou alone shalt bear it.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 The foolish woman is clamorous; she is stupid, and knoweth nothing.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 And she sitteth at the entry of her house, on a seat in the high places of the city,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 to call passers-by who go right on their ways:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Whoso is simple, let him turn in hither. And to him that is void of understanding she saith,
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Stolen waters are sweet, and the bread of secrecy is pleasant.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 But he knoweth not that the dead are there; [that] her guests are in the depths of Sheol. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )