< Proverbs 6 >

1 My son, if thou hast become surety for thy friend, if thou hast stricken thy hand for a stranger,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 thou art snared with the words of thy mouth, thou art taken with the words of thy mouth.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Do this now, my son, and deliver thyself, since thou hast come into the hand of thy friend: go, humble thyself, and be urgent with thy friend.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Give not sleep to thine eyes, nor slumber to thine eyelids:
Usagone tulo, usawodzere.
5 deliver thyself as a gazelle from the hand [of the hunter], and as a bird from the hand of the fowler.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Go to the ant, thou sluggard; consider her ways and be wise:
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 which having no chief, overseer, or ruler,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 provideth her bread in the summer, [and] gathereth her food in the harvest.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 How long, sluggard, wilt thou lie down? When wilt thou arise out of thy sleep?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 A little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to rest!
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 So shall thy poverty come as a roving plunderer, and thy penury as an armed man.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 A man of Belial, a wicked person, is he that goeth about with a perverse mouth;
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 he winketh with his eyes, he speaketh with his feet, he teacheth with his fingers;
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 deceits are in his heart; he deviseth mischief at all times, he soweth discords.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Therefore shall his calamity come suddenly: in a moment shall he be broken, and without remedy.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 These six [things] doth Jehovah hate, yea, seven are an abomination unto him:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 haughty eyes, a lying tongue, and hands that shed innocent blood;
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 a heart that deviseth wicked imaginations; feet that are swift in running to mischief;
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 a false witness that uttereth lies, and he that soweth discords among brethren.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 My son, observe thy father's commandment, and forsake not the teaching of thy mother;
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 bind them continually upon thy heart, tie them about thy neck:
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 when thou walkest, it shall lead thee; when thou sleepest, it shall keep thee; and [when] thou awakest, it shall talk with thee.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 For the commandment is a lamp, and the teaching a light, and reproofs of instruction are the way of life:
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 to keep thee from the evil woman, from the flattery of the tongue of a strange woman.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Lust not after her beauty in thy heart, neither let her take thee with her eyelids;
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 for by means of a whorish woman [a man is brought] to a loaf of bread, and another's wife doth hunt for the precious soul.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Can a man take fire in his bosom, and his garments not be burned?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Can one go upon hot coals, and his feet not be scorched?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 So he that goeth in to his neighbour's wife: whosoever toucheth her shall not be innocent.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 They do not despise a thief, if he steal to satisfy his soul when he is hungry:
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 and if he be found, he shall restore sevenfold; he shall give all the substance of his house.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Whoso committeth adultery with a woman is void of understanding: he that doeth it destroyeth his own soul.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 A wound and contempt shall he get; and his reproach shall not be wiped away.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 For jealousy is the rage of a man, and he will not spare in the day of vengeance;
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 he will not regard any ransom, neither will he rest content though thou multipliest [thy] gifts.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Proverbs 6 >