< Proverbs 26 >

1 As snow in summer, and as rain in harvest, so honour beseemeth not a fool.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 As the sparrow for flitting about, as the swallow for flying, so a curse undeserved shall not come.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 A whip for the horse, a bridle for the ass, and a rod for the back of fools.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Answer not a fool according to his folly, lest thou also be like unto him.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Answer a fool according to his folly, lest he be wise in his own eyes.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 He that sendeth a message by the hand of a fool cutteth off [his own] feet, [and] drinketh damage.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 The legs of the lame hang loose; so is a proverb in the mouth of fools.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 As a bag of gems in a stoneheap, so is he that giveth honour to a fool.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 [As] a thorn goeth up into the hand of a drunkard, so is a proverb in the mouth of fools.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 A master roughly worketh every one: he both hireth the fool and hireth passers-by.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 As a dog turneth back to its vomit, [so] a fool repeateth his folly.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Hast thou seen a man wise in his own eyes? There is more hope of a fool than of him.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 The sluggard saith, There is a fierce lion in the way; a lion is in the midst of the streets!
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 [As] the door turneth upon its hinges, so the sluggard upon his bed.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 The sluggard burieth his hand in the dish: it wearieth him to bring it again to his mouth.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 A sluggard is wiser in his own eyes than seven [men] that answer discreetly.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 He that passing by vexeth himself with strife belonging not to him, is [like] one that taketh a dog by the ears.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 As a madman who casteth firebrands, arrows, and death,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 so is a man that deceiveth his neighbour, and saith, Am I not in sport?
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Where no wood is, the fire goeth out; and where there is no talebearer, the contention ceaseth.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 [As] coals for hot coals, and wood for fire, so is a contentious man to inflame strife.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 The words of a talebearer are as dainty morsels, and they go down into the innermost parts of the belly.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Ardent lips, and a wicked heart, are [as] an earthen vessel overlaid with silver dross.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 He that hateth dissembleth with his lips, but he layeth up deceit within him:
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 when his voice is gracious, believe him not, for there are seven abominations in his heart.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Though [his] hatred is covered by dissimulation, his wickedness shall be made manifest in the congregation.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Whoso diggeth a pit shall fall therein; and he that rolleth a stone, it shall return upon him.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 A lying tongue hateth those that are injured by it, and a flattering mouth worketh ruin.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbs 26 >