< Proverbs 17 >
1 Better is a dry morsel, and quietness therewith, than a house full of feasting [with] strife.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 A wise servant shall rule over a son that causeth shame, and shall have part in the inheritance among the brethren.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 The fining-pot is for silver, and the furnace for gold; but Jehovah trieth the hearts.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 The evil-doer giveth heed to iniquitous lips; the liar giveth ear to a mischievous tongue.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Whoso mocketh a poor [man] reproacheth his Maker; he that is glad at calamity shall not be held innocent.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Children's children are the crown of old men; and the glory of children are their fathers.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Excellent speech becometh not a vile [man]; how much less do lying lips a noble!
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 A gift is a precious stone in the eyes of the possessor: whithersoever it turneth it prospereth.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 He that covereth transgression seeketh love; but he that bringeth a matter up again separateth very friends.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 A reproof entereth more deeply into him that hath understanding than a hundred stripes into a fool.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 An evil [man] seeketh only rebellion; but a cruel messenger shall be sent against him.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Let a bear robbed of her whelps meet a man rather than a fool in his folly.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Whoso rewardeth evil for good, evil shall not depart from his house.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 The beginning of contention is [as] when one letteth out water; therefore leave off strife before it become vehement.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 He that justifieth the wicked, and he that condemneth the righteous, even they both are abomination to Jehovah.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 To what purpose is there a price in the hand of a fool to get wisdom, seeing [he] hath no sense?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 The friend loveth at all times, and a brother is born for adversity.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 A senseless man striketh hands, becoming surety for his neighbour.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 He loveth transgression that loveth a quarrel; he that maketh high his gate seeketh destruction.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 He that hath a perverse heart findeth no good; and he that shifteth about with his tongue falleth into evil.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 He that begetteth a fool [doeth it] to his sorrow, and the father of a vile [man] hath no joy.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 A joyful heart promoteth healing; but a broken spirit drieth up the bones.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 A wicked [man] taketh a gift out of the bosom, to pervert the paths of judgment.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Wisdom is before him that hath understanding; but the eyes of a fool are in the ends of the earth.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 A foolish son is a grief to his father, and bitterness to her that bore him.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 To punish a righteous [man] is not good, nor to strike nobles because of [their] uprightness.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 He that hath knowledge spareth his words; and a man of understanding is of a cool spirit.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Even a fool when he holdeth his peace is reckoned wise, [and] he that shutteth his lips, intelligent.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.