< Proverbs 16 >

1 The purposes of the heart are of man, but the answer of the tongue is from Jehovah.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All the ways of a man are clean in his own eyes; but Jehovah weigheth the spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Commit thy works unto Jehovah, and thy thoughts shall be established.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Jehovah hath wrought everything on his own account, yea, even the wicked for the day of evil.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Every proud heart is an abomination to Jehovah: hand for hand, he shall not be held innocent.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 By loving-kindness and truth iniquity is atoned for; and by the fear of Jehovah [men] depart from evil.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When a man's ways please Jehovah, he maketh even his enemies to be at peace with him.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better is a little with righteousness, than great revenues without right.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 The heart of man deviseth his way, but Jehovah directeth his steps.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 An oracle is on the lips of the king: his mouth will not err in judgment.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 The just balance and scales are Jehovah's; all the weights of the bag are his work.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 It is an abomination to kings to commit wickedness; for the throne is established by righteousness.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Righteous lips are the delight of kings, and they love him that speaketh aright.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 The fury of a king is [as] messengers of death; but a wise man will pacify it.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the light of the king's countenance is life, and his favour is as a cloud of the latter rain.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 How much better is it to get wisdom than fine gold, and the getting of intelligence to be preferred to silver!
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 The highway of the upright is to depart from evil: he that taketh heed to his way keepeth his soul.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pride [goeth] before destruction, and a haughty spirit before a fall.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Better is it to be of a humble spirit with the meek, than to divide the spoil with the proud.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 He that giveth heed to the word shall find good; and whoso confideth in Jehovah, happy is he.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 The wise in heart is called intelligent, and the sweetness of the lips increaseth learning.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Wisdom is a fountain of life for him that hath it; but the instruction of fools is folly.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of the wise maketh his mouth intelligent, and upon his lips increaseth learning.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Pleasant words are [as] a honeycomb, sweet to the soul, and health for the bones.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way that seemeth right unto a man, but the end thereof is the ways of death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 The appetite of the labourer laboureth for him, for his mouth urgeth him on.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 A man of Belial diggeth up evil, and on his lips there is as a scorching fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A false man soweth contention; and a talebearer separateth very friends.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 A violent man enticeth his neighbour, and leadeth him into a way that is not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 He that shutteth his eyes, [it is] to devise froward things; biting his lips, he bringeth evil to pass.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 The hoary head is a crown of glory, [if] it is found in the way of righteousness.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 He that is slow to anger is better than the mighty, and he that ruleth his spirit than he that taketh a city.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 The lot is cast into the lap; but the whole decision is of Jehovah.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbs 16 >