< Proverbs 10 >
1 The Proverbs of Solomon. A wise son maketh a glad father; but a foolish son is the grief of his mother.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Treasures of wickedness profit nothing; but righteousness delivereth from death.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Jehovah suffereth not the soul of the righteous [man] to famish; but he repelleth the craving of the wicked.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 He cometh to want that dealeth with a slack hand; but the hand of the diligent maketh rich.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 He that gathereth in summer is a wise son; he that sleepeth in harvest is a son that causeth shame.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Blessings are upon the head of a righteous [man]; but the mouth of the wicked covereth violence.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 The memory of the righteous [man] shall be blessed; but the name of the wicked shall rot.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 The wise in heart receiveth commandments; but a prating fool shall fall.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 He that walketh in integrity walketh securely; but he that perverteth his ways shall be known.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 He that winketh with the eye causeth grief, and a prating fool shall fall.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 The mouth of a righteous [man] is a fountain of life; but the mouth of the wicked covereth violence.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Hatred stirreth up strifes; but love covereth all transgressions.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 In the lips of an intelligent [man] wisdom is found; but a rod is for the back of him that is void of understanding.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 The wise lay up knowledge; but the mouth of the fool is near destruction.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 The rich man's wealth is his strong city; the destruction of the poor is their poverty.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 The labour of a righteous [man] [tendeth] to life; the revenue of a wicked [man], to sin.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Keeping instruction is the path to life; but he that forsaketh reproof goeth astray.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 He that covereth hatred hath lying lips, and he that sendeth forth a slander is a fool.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 In the multitude of words there wanteth not transgression; but he that restraineth his lips doeth wisely.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 The tongue of the righteous [man] is [as] choice silver; the heart of the wicked is little worth.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 The lips of a righteous [man] feed many; but fools die for want of understanding.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 The blessing of Jehovah, it maketh rich, and he addeth no sorrow to it.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 It is as sport to a foolish [man] to do wickedness; but a man of understanding hath wisdom.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 The fear of a wicked [man], it shall come upon him; but the desire of the righteous shall be granted.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 As a whirlwind passeth, so is the wicked no [more]; but the righteous is an everlasting foundation.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 As vinegar to the teeth, and as smoke to the eyes, so is the sluggard to them that send him.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 The fear of Jehovah prolongeth days; but the years of the wicked shall be shortened.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 The hope of the righteous is joy; but the expectation of the wicked shall perish.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 The way of Jehovah is strength to the perfect [man], but destruction to the workers of iniquity.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 The righteous [man] shall never be moved; but the wicked shall not inhabit the land.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 The mouth of a righteous [man] putteth forth wisdom; but the froward tongue shall be cut out.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 The lips of a righteous [man] know what is acceptable; but the mouth of the wicked is frowardness.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.