< Numbers 13 >

1 And Jehovah spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Send thou men, that they may search out the land of Canaan, which I give unto the children of Israel. Ye shall send a man of every tribe of his fathers, each a prince among them.
“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
3 And Moses sent them from the wilderness of Paran: according to the commandment of Jehovah, all of them heads of the children of Israel.
Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
4 And these are their names: for the tribe of Reuben, Shammua the son of Zaccur;
Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
5 for the tribe of Simeon, Shaphat the son of Hori;
kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
6 for the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh;
kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
7 for the tribe of Issachar, Igal the son of Joseph;
kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
8 for the tribe of Ephraim, Hoshea the son of Nun;
kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
9 for the tribe of Benjamin, Palti the son of Raphu;
kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
10 for the tribe of Zebulun, Gaddiel the son of Sodi;
kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
11 for the tribe of Joseph, for the tribe of Manasseh, Gaddi the son of Susi;
kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
12 for the tribe of Dan, Ammiel the son of Gemalli;
kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
13 for the tribe of Asher, Sethur the son of Michael;
kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
14 for the tribe of Naphtali, Nahbi the son of Vophsi;
kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
15 for the tribe of Gad, Geuel the son of Machi.
kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
16 These are the names of the men whom Moses sent to search out the land. And Moses called Hoshea the son of Nun, Jehoshua.
Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
17 And Moses sent them to search out the land of Canaan, and said to them, Go up this way by the south and go up into the hill-country,
Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
18 and ye shall see the land, what it is; and the people that dwell in it, whether they are strong or weak, few or many;
Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
19 and what the land is that they dwell in, whether it is good or bad; and what cities they are that they dwell in, whether in camps, or in strongholds;
Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
20 and what the land is, whether it is fat or lean, whether there are trees in it, or not. And take courage, and bring of the fruit of the land. Now the time was the time of the first grapes.
Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
21 And they went up, and searched out the land from the wilderness of Zin to Rehob, where one comes towards Hamath.
Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
22 And they went up by the south, and came to Hebron; and Ahiman, Sheshai, and Talmai, the children of Anak, were there. Now Hebron had been built seven years before Zoan in Egypt.
Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
23 And they came as far as the valley of Eshcol, and cut down thence a branch with one bunch of grapes, and they bore it between two upon a pole; and [they brought] of the pomegranates, and of the figs.
Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
24 That place was called the valley of Eshcol, because of the grapes which the children of Israel had cut down there.
Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
25 And they returned from searching out the land after forty days.
Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
26 And they came, and went to Moses and to Aaron, and to the whole assembly of the children of Israel, to the wilderness of Paran, to Kadesh; and brought back word to them, and to the whole assembly; and shewed them the fruit of the land.
Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
27 And they told him, and said, We came to the land to which thou didst send us, and surely it floweth with milk and honey; and this is the fruit of it.
Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
28 Only, the people are strong that dwell in the land, and the cities are walled, very great; moreover we saw the children of Anak there.
Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
29 Amalek dwells in the land of the south; and the Hittites, and the Jebusites, and the Amorites dwell in the hill-country; and the Canaanites dwell by the sea, and by the side of the Jordan.
Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
30 And Caleb stilled the people before Moses, and said, Let us go up boldly and possess it, for we are well able to do it.
Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
31 But the men that went up with him said, We are not able to go up against the people, for they are stronger than we.
Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
32 And they brought to the children of Israel an evil report of the land which they had searched out, saying, The land, which we have passed through to search it out, is a land that eateth up its inhabitants; and all the people that we have seen in it are men of great stature;
Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
33 and there have we seen giants — the sons of Anak are of the giants — and we were in our sight as grasshoppers, and so we were also in their sight.
Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”

< Numbers 13 >