< Matthew 5 >

1 But seeing the crowds, he went up into the mountain, and having sat down, his disciples came to him;
Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
2 and, having opened his mouth, he taught them, saying,
ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
3 Blessed [are] the poor in spirit, for theirs is the kingdom of the heavens.
“Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
4 Blessed they that mourn, for they shall be comforted.
Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
5 Blessed the meek, for they shall inherit the earth.
Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
6 Blessed they who hunger and thirst after righteousness, for they shall be filled.
Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
7 Blessed the merciful, for they shall find mercy.
Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
8 Blessed the pure in heart, for they shall see God.
Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
9 Blessed the peace-makers, for they shall be called sons of God.
Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
10 Blessed they who are persecuted on account of righteousness, for theirs is the kingdom of the heavens.
Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
11 Blessed are ye when they may reproach and persecute you, and say every wicked thing against you, lying, for my sake.
“Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
12 Rejoice and exult, for your reward is great in the heavens; for thus have they persecuted the prophets who were before you.
Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
13 Ye are the salt of the earth; but if the salt have become insipid, wherewith shall it be salted? It is no longer fit for anything but to be cast out and to be trodden under foot by men.
“Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
14 Ye are the light of the world: a city situated on the top of a mountain cannot be hid.
“Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
15 Nor do [men] light a lamp and put it under the bushel, but upon the lamp-stand, and it shines for all who are in the house.
Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
16 Let your light thus shine before men, so that they may see your upright works, and glorify your Father who is in the heavens.
Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
17 Think not that I am come to make void the law or the prophets; I am not come to make void, but to fulfil.
“Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
18 For verily I say unto you, Until the heaven and the earth pass away, one iota or one tittle shall in no wise pass from the law till all come to pass.
Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
19 Whosoever then shall do away with one of these least commandments, and shall teach men so, shall be called least in the kingdom of the heavens; but whosoever shall practise and teach [them], he shall be called great in the kingdom of the heavens.
Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
20 For I say unto you, that unless your righteousness surpass [that] of the scribes and Pharisees, ye shall in no wise enter into the kingdom of the heavens.
Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
21 Ye have heard that it was said to the ancients, Thou shalt not kill; but whosoever shall kill shall be subject to the judgment.
“Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
22 But I say unto you, that every one that is lightly angry with his brother shall be subject to the judgment; but whosoever shall say to his brother, Raca, shall be subject to [be called before] the sanhedrim; but whosoever shall say, Fool, shall be subject to the penalty of the hell of fire. (Geenna g1067)
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna g1067)
23 If therefore thou shouldest offer thy gift at the altar, and there shouldest remember that thy brother has something against thee,
“Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
24 leave there thy gift before the altar, and first go, be reconciled to thy brother, and then come and offer thy gift.
usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
25 Make friends with thine adverse party quickly, whilst thou art in the way with him; lest some time the adverse party deliver thee to the judge, and the judge deliver thee to the officer, and thou be cast into prison.
“Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
26 Verily I say to thee, Thou shalt in no wise come out thence till thou hast paid the last farthing.
Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
27 Ye have heard that it has been said, Thou shalt not commit adultery.
“Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
28 But I say unto you, that every one who looks upon a woman to lust after her has already committed adultery with her in his heart.
Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
29 But if thy right eye be a snare to thee, pluck it out and cast it from thee: for it is profitable for thee that one of thy members perish, and not thy whole body be cast into hell. (Geenna g1067)
Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
30 And if thy right hand be a snare to thee, cut it off and cast it from thee: for it is profitable for thee that one of thy members perish, and not thy whole body be cast into hell. (Geenna g1067)
Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
31 It has been said too, Whosoever shall put away his wife, let him give her a letter of divorce.
“Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
32 But I say unto you, that whosoever shall put away his wife, except for cause of fornication, makes her commit adultery, and whosoever marries one that is put away commits adultery.
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
33 Again, ye have heard that it has been said to the ancients, Thou shalt not forswear thyself, but shalt render to the Lord what thou hast sworn.
“Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
34 But I say unto you, Do not swear at all; neither by the heaven, because it is [the] throne of God;
Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
35 nor by the earth, because it is [the] footstool of his feet; nor by Jerusalem, because it is [the] city of the great King.
Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
36 Neither shalt thou swear by thy head, because thou canst not make one hair white or black.
Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
37 But let your word be Yea, yea; Nay, nay; but what is more than these is from evil.
Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
38 Ye have heard that it has been said, Eye for eye and tooth for tooth.
“Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
39 But I say unto you, not to resist evil; but whoever shall strike thee on thy right cheek, turn to him also the other;
Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
40 and to him that would go to law with thee and take thy body coat, leave him thy cloak also.
Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
41 And whoever will compel thee to go one mile, go with him two.
Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
42 To him that asks of thee give, and from him that desires to borrow of thee turn not away.
Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
43 Ye have heard that it has been said, Thou shalt love thy neighbour and hate thine enemy.
“Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
44 But I say unto you, Love your enemies, [bless those who curse you, ] do good to those who hate you, and pray for those who [insult you and] persecute you,
Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
45 that ye may be [the] sons of your Father who is in [the] heavens; for he makes his sun rise on evil and good, and sends rain on just and unjust.
kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
46 For if ye should love those who love you, what reward have ye? Do not also the tax-gatherers the same?
Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
47 And if ye should salute your brethren only, what do ye extraordinary? Do not also the Gentiles the same?
Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
48 Be ye therefore perfect as your heavenly Father is perfect.
Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”

< Matthew 5 >