< Leviticus 8 >

1 And Jehovah spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Take Aaron and his sons with him, and the garments and the anointing oil, and the bullock of the sin-offering, and the two rams, and the basket of unleavened [bread];
“Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
3 and gather all the assembly together at the entrance of the tent of meeting.
ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
4 And Moses did as Jehovah had commanded him; and the assembly was collected at the entrance of the tent of meeting.
Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
5 And Moses said to the assembly, This is the thing which Jehovah has commanded to be done.
Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
6 And Moses brought Aaron near, and his sons, and bathed them with water.
Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
7 And he put upon him the vest and girded him with the girdle, and clothed him with the cloak, and put the ephod on him, and he girded him with the girdle of the ephod, and fastened the ephod on him.
Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
8 And he put the breastplate on it, and put on the breastplate the Urim and the Thummim;
Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
9 and he put the turban upon his head; and upon the turban, on the front of it, he put the golden plate, the holy diadem; as Jehovah had commanded Moses.
Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
10 And Moses took the anointing oil, and anointed the tabernacle and all that was in it, and hallowed them.
Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
11 And he sprinkled thereof on the altar seven times, and anointed the altar and all its utensils, and the laver and its stand, to hallow them.
Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
12 And he poured of the anointing oil on Aaron's head, and anointed him, to hallow him.
Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
13 And Moses brought Aaron's sons near and clothed them with the vests, and girded them with the girdles, and bound the high caps on them, as Jehovah had commanded Moses.
Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 And he brought near the bullock for the sin-offering; and Aaron and his sons laid their hands on the head of the bullock for the sin-offering;
Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
15 and he slaughtered [it], and Moses took the blood, and put [it] on the horns of the altar round about with his finger, and cleansed the altar from sin, and the blood he poured at the bottom of the altar, and hallowed it, making atonement for it.
Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
16 And he took all the fat that was on the inwards, and the net of the liver, and the two kidneys, and their fat, and Moses burned [them] on the altar.
Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
17 And the bullock, and its skin, and its flesh, and its dung he burned with fire outside the camp, as Jehovah had commanded Moses.
Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
18 And he presented the ram of the burnt-offering; and Aaron and his sons laid their hands on the head of the ram;
Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
19 and he slaughtered [it]; and Moses sprinkled the blood on the altar round about.
Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
20 And the ram he cut up into its pieces; and Moses burned the head, and the pieces, and the fat;
Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
21 and the inwards and the legs he washed in water; and Moses burned the whole ram on the altar: it was a burnt-offering for a sweet odour, it was an offering by fire to Jehovah; as Jehovah had commanded Moses.
Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
22 And he presented the second ram, the ram of consecration; and Aaron and his sons laid their hands on the head of the ram;
Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
23 and one slaughtered [it]; and Moses took of its blood, and put [it] on the tip of Aaron's right ear, and on the thumb of his right hand, and on the great toe of his right foot;
Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
24 and he brought Aaron's sons near, and Moses put of the blood on the tip of their right ear, and on the thumb of their right hand, and on the great toe of their right foot; and Moses sprinkled the blood upon the altar round about.
Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
25 And he took the fat, and the fat tail, and all the fat that was on the inwards, and the net of the liver, and the two kidneys and their fat, and the right shoulder;
Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
26 and out of the basket of unleavened bread that was before Jehovah he took one unleavened cake, and a cake of oiled bread, and one wafer, and put them on the fat and upon the right shoulder;
Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
27 and he gave all into Aaron's hands, and into his sons' hands, and waved them as a wave-offering before Jehovah.
Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
28 And Moses took them from off their hands, and burned [them] on the altar, over the burnt-offering: they were a consecration-offering for a sweet odour: it was an offering by fire to Jehovah.
Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
29 And Moses took the breast, and waved it as a wave-offering before Jehovah; of the ram of consecration it was Moses' part; as Jehovah had commanded Moses.
Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
30 And Moses took of the anointing oil, and of the blood that was on the altar, and sprinkled [it] on Aaron, on his garments, and on his sons, and on his sons' garments with him; and hallowed Aaron, his garments, and his sons, and his sons' garments with him.
Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
31 And Moses spoke to Aaron and to his sons, Boil the flesh at the entrance of the tent of meeting; and there eat it and the bread that is in the basket of the consecration-offering, as I commanded, saying, Aaron and his sons shall eat it.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
32 And that which remaineth of the flesh and of the bread shall ye burn with fire.
Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
33 And ye shall not go out from the entrance of the tent of meeting seven days, until the day when the days of your consecration are at an end: for seven days shall ye be consecrated.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
34 As he hath done this day, [so] Jehovah hath commanded to do, to make atonement for you.
Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
35 And ye shall abide at the entrance of the tent of meeting day and night seven days, and keep the charge of Jehovah, that ye die not; for so I am commanded.
Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
36 And Aaron and his sons did all things that Jehovah had commanded by the hand of Moses.
Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.

< Leviticus 8 >