< Joshua 7 >

1 But the children of Israel committed unfaithfulness in that which had been brought under the curse: Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerah, of the tribe of Judah, took of the accursed thing; and the anger of Jehovah was kindled against the children of Israel.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 And Joshua sent men from Jericho to Ai, which is beside Beth-Aven, on the east side of Bethel, and spoke to them, saying, Go up and spy out the country. And the men went up and spied out Ai.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 And they returned to Joshua, and said to him, Let not all the people go up; let about two or three thousand men go up and smite Ai; make not all the people to toil thither, for they are few.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 And there went up thither of the people about three thousand men, but they fled before the men of Ai.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 And the men of Ai smote of them about thirty-six men; and they pursued them from before the gate to Shebarim, and smote them on the descent. Then the hearts of the people melted, and became as water.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 And Joshua rent his clothes, and fell to the earth upon his face before the ark of Jehovah until the evening, he and the elders of Israel, and threw dust upon their heads.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 And Joshua said, Alas, Lord Jehovah, wherefore hast thou at all brought this people over the Jordan, to deliver us into the hand of the Amorites, to destroy us? Oh that we had been content and had remained beyond the Jordan!
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 Ah Lord! what shall I say after Israel have turned their backs before their enemies?
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 When the Canaanites and all the inhabitants of the land shall hear [of it], they will surround us, and cut off our name from the earth. And what wilt thou do unto thy great name?
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 And Jehovah said to Joshua, Rise up; wherefore liest thou thus upon thy face?
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 Israel hath sinned, and they have also transgressed my covenant which I commanded them, and they have even taken of the accursed thing, and have also stolen, and dissembled also, and they have put it among their stuff.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 And the children of Israel shall not be able to stand before their enemies: they shall turn their backs before their enemies, for they have made themselves accursed. I will no more be with you, except ye destroy the accursed thing from your midst.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Rise up, hallow the people, and say, Hallow yourselves for to-morrow; for thus saith Jehovah the God of Israel, There is an accursed thing in the midst of thee, Israel: thou shalt not be able to stand before thine enemies, until ye take away the accursed thing from your midst.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 And ye shall be brought near in the morning according to your tribes; and it shall be, that the tribe which Jehovah taketh shall come forward by families, and the family which Jehovah taketh shall come forward by households; and the household which Jehovah taketh shall come forward man by man.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 And it shall be, that he who is taken with the accursed thing shall be burned with fire, he and all that he hath, because he hath transgressed the covenant of Jehovah, and because he hath wrought wickedness in Israel.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 And Joshua rose early in the morning, and caused Israel to come forward by their tribes, and the tribe of Judah was taken.
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 And he caused the families of Judah to come forward, and he took the family of the Zarhites. And he caused the family of the Zarhites to come forward man by man, and Zabdi was taken.
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 And he caused his household to come forward man by man, and Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerah, of the tribe of Judah, was taken.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 And Joshua said to Achan, My son, give, I pray thee, glory to Jehovah the God of Israel, and make confession to him: tell me now what thou hast done, keep it not back from me.
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 And Achan answered Joshua and said, Indeed I have sinned against Jehovah the God of Israel, and thus and thus have I done.
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 I saw among the spoils a beautiful mantle of Shinar, and two hundred shekels of silver, and a golden bar of fifty shekels weight, and I coveted them and took them; and behold, they are hid in the earth in the midst of my tent, and the silver under it.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 And Joshua sent messengers, and they ran to the tent, and behold, it was hid in his tent, and the silver under it.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 And they took them out of the midst of the tent, and brought them to Joshua and to all the children of Israel, and laid them out before Jehovah.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 Then Joshua, and all Israel with him, took Achan the son of Zerah, and the silver, and the mantle, and the bar of gold, and his sons, and his daughters, and his oxen, and his asses, and his sheep, and his tent, and all that he had; and they brought them up into the valley of Achor.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 And Joshua said, How hast thou troubled us! Jehovah will trouble thee this day. And all Israel stoned him with stones; and they burned them with fire, and stoned them with stones.
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 And they raised over him a great heap of stones, [which is there] to this day. And Jehovah turned from the fierceness of his anger. Therefore the name of that place was called, The Valley of Achor, to this day.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.

< Joshua 7 >