< Joshua 21 >
1 Then the chief fathers of the Levites drew near to Eleazar the priest, and to Joshua the son of Nun, and to the chief fathers of the tribes of the children of Israel;
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 and they spoke to them at Shiloh in the land of Canaan, saying, Jehovah commanded through Moses to give us cities to dwell in, and their suburbs for our cattle.
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 And the children of Israel gave to the Levites out of their inheritance, according to the word of Jehovah, these cities and their suburbs.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 And the lot came forth for the families of the Kohathites. And the children of Aaron the priest, of the Levites, had by lot out of the tribe of Judah, and out of the tribe of the Simeonites, and out of the tribe of Benjamin, thirteen cities.
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 And the children of Kohath that remained had by lot out of the families of the tribe of Ephraim, and out of the tribe of Dan, and out of the half tribe of Manasseh, ten cities.
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 And the children of Gershon had by lot out of the families of the tribe of Issachar, and out of the tribe of Asher, and out of the tribe of Naphtali, and out of the half tribe of Manasseh in Bashan, thirteen cities.
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 The children of Merari according to their families had by lot out of the tribe of Reuben, and out of the tribe of Gad, and out of the tribe of Zebulun, twelve cities.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 And the children of Israel gave by lot to the Levites these cities and their suburbs, as Jehovah commanded through Moses.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 And they gave out of the tribe of the children of Judah, and out of the tribe of the children of Simeon, these cities which were mentioned by name,
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 and which the children of Aaron, of the families of the Kohathites, of the children of Levi had (for theirs was the first lot);
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 and they gave them Kirjath-Arba, [which Arba was] the father of Anak, that is, Hebron, in the mountain of Judah, with its suburbs round about it.
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 But the fields of the city and the hamlets thereof gave they to Caleb the son of Jephunneh for his possession.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 And they gave to the children of Aaron the priest the city of refuge for the slayer, Hebron and its suburbs; and Libnah and its suburbs,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
14 and Jattir and its suburbs, and Eshtemoa and its suburbs,
Yatiri, Esitemowa,
15 and Holon and its suburbs, and Debir and its suburbs,
Holoni, Debri,
16 and Ain and its suburbs, and Juttah and its suburbs, [and] Beth-shemesh and its suburbs: nine cities out of those two tribes;
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 and out of the tribe of Benjamin: Gibeon and its suburbs, Geba and its suburbs,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Anathoth and its suburbs, and Almon and its suburbs; four cities.
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 All the cities of the children of Aaron, the priests, were thirteen cities and their suburbs.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 And to the families of the children of Kohath, the Levites that remained of the children of Kohath, [they gave cities]. And the cities of their lot were out of the tribe of Ephraim,
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 and they gave them the city of refuge for the slayer, Shechem and its suburbs in mount Ephraim; and Gezer and its suburbs,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 and Kibzaim and its suburbs, and Beth-horon and its suburbs: four cities;
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 and out of the tribe of Dan, Eltekeh and its suburbs, Gibbethon and its suburbs,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Ajalon and its suburbs, Gath-Rimmon and its suburbs: four cities;
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 and out of half the tribe of Manasseh, Taanach and its suburbs and Gath-Rimmon and its suburbs: two cities.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 All the cities were ten and their suburbs, for the families of the children of Kohath that remained.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 And to the children of Gershon, of the families of the Levites, out of half the tribe of Manasseh, [they gave] the city of refuge for the slayer, Golan in Bashan and its suburbs; and Beeshterah and its suburbs: two cities;
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 and out of the tribe of Issachar, Kishion and its suburbs, Dabrath and its suburbs,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Jarmuth and its suburbs, En-gannim and its suburbs: four cities;
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 and out of the tribe of Asher, Mishal and its suburbs, Abdon and its suburbs,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Helkath and its suburbs, and Rehob and its suburbs: four cities;
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 and out of the tribe of Naphtali, the city of refuge for the slayer, Kedesh in Galilee, and its suburbs; and Hammoth-Dor and its suburbs, and Kartan and its suburbs: three cities.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 All the cities of the Gershonites according to their families were thirteen cities and their suburbs.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 And to the families of the children of Merari, that remained of the Levites, [they gave] out of the tribe of Zebulun, Jokneam and its suburbs, Kartah and its suburbs,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
35 Dimnah and its suburbs, Nahalal and its suburbs: four cities;
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 and out of the tribe of Reuben, Bezer and its suburbs, and Jahzah and its suburbs,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Kedemoth and its suburbs, and Mephaath and its suburbs: four cities;
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 and out of the tribe of Gad, the city of refuge for the slayer, Ramoth in Gilead and its suburbs; and Mahanaim and its suburbs,
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Heshbon and its suburbs, Jaazer and its suburbs: four cities in all.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 [These were] all the cities of the children of Merari according to their families, which remained of the families of the Levites, and their lot was twelve cities.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 All the cities of the Levites within the possession of the children of Israel were forty-eight cities and their suburbs.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 Each one of these cities had its suburbs round about it: thus were all these cities.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 And Jehovah gave to Israel all the land which he swore to give unto their fathers; and they took possession of it, and dwelt in it.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 And Jehovah gave them rest round about, according to all that he had sworn unto their fathers; and there stood not a man of all their enemies before them: Jehovah gave all their enemies into their hand.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 There failed nothing of all the good things that Jehovah had spoken to the house of Israel: all came to pass.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.