< John 7 >

1 And after these things Jesus walked in Galilee, for he would not walk in Judaea, because the Jews sought to kill him.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Now the tabernacles, the feast of the Jews, was near.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 His brethren therefore said to him, Remove hence and go into Judaea, that thy disciples also may see thy works which thou doest;
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 for no one does anything in secret and himself seeks to be [known] in public. If thou doest these things, manifest thyself to the world:
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 for neither did his brethren believe on him.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Jesus therefore says to them, My time is not yet come, but your time is always ready.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 The world cannot hate you, but me it hates, because I bear witness concerning it that its works are evil.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Ye, go ye up to this feast. I go not up to this feast, for my time is not yet fulfilled.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 Having said these things to them he abode in Galilee.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 But when his brethren had gone up, then he himself also went up to the feast, not openly, but as in secret.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 The Jews therefore sought him at the feast, and said, Where is he?
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 And there was much murmuring concerning him among the crowds. Some said, He is [a] good [man]; others said, No; but he deceives the crowd.
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 However, no one spoke openly concerning him on account of [their] fear of the Jews.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 But when it was now the middle of the feast, Jesus went up into the temple and taught.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 The Jews therefore wondered, saying, How knows this [man] letters, having never learned?
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Jesus therefore answered them and said, My doctrine is not mine, but [that] of him that has sent me.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 If any one desire to practise his will, he shall know concerning the doctrine, whether it is of God, or [that] I speak from myself.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 He that speaks from himself seeks his own glory; but he that seeks the glory of him that has sent him, he is true, and unrighteousness is not in him.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Has not Moses given you the law, and no one of you practises the law? Why do ye seek to kill me?
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 The crowd answered [and said], Thou hast a demon: who seeks to kill thee?
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Jesus answered and said to them, I have done one work, and ye all wonder.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Therefore Moses gave you circumcision (not that it is of Moses, but of the fathers), and ye circumcise a man on sabbath.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 If a man receives circumcision on sabbath, that the law of Moses may not be violated, are ye angry with me because I have made a man entirely sound on sabbath?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Judge not according to sight, but judge righteous judgment.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Some therefore of those of Jerusalem said, Is not this he whom they seek to kill?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 and behold, he speaks openly, and they say nothing to him. Have the rulers then indeed recognised that this is the Christ?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 But [as to] this [man] we know whence he is. Now [as to] the Christ, when he comes, no one knows whence he is.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Jesus therefore cried out in the temple, teaching and saying, Ye both know me and ye know whence I am; and I am not come of myself, but he that sent me is true, whom ye do not know.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 I know him, because I am from him, and he has sent me.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 They sought therefore to take him; and no one laid his hand upon him, because his hour had not yet come.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 But many of the crowd believed on him, and said, Will the Christ, when he comes, do more signs than those which this [man] has done?
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 The Pharisees heard the crowd murmuring these things concerning him, and the Pharisees and the chief priests sent officers that they might take him.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Jesus therefore said, Yet a little while I am with you, and I go to him that has sent me.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Ye shall seek me and shall not find [me], and where I am ye cannot come.
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 The Jews therefore said to one another, Where is he about to go that we shall not find him? Is he about to go to the dispersion among the Greeks, and teach the Greeks?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 What word is this which he said, Ye shall seek me and shall not find [me]; and where I am ye cannot come?
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 In the last, the great day of the feast, Jesus stood and cried saying, If any one thirst, let him come to me and drink.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 He that believes on me, as the scripture has said, out of his belly shall flow rivers of living water.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 But this he said concerning the Spirit, which they that believed on him were about to receive; for [the] Spirit was not yet, because Jesus had not yet been glorified.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 [Some] out of the crowd therefore, having heard this word, said, This is truly the prophet.
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Others said, This is the Christ. Others said, Does then the Christ come out of Galilee?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Has not the scripture said that the Christ comes of the seed of David, and from the village of Bethlehem, where David was?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 There was a division therefore in the crowd on account of him.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 But some of them desired to take him, but no one laid hands upon him.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 The officers therefore came to the chief priests and Pharisees, and they said to them, Why have ye not brought him?
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 The officers answered, Never man spoke thus, as this man [speaks].
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 The Pharisees therefore answered them, Are ye also deceived?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Has any one of the rulers believed on him, or of the Pharisees?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 But this crowd, which does not know the law, are accursed.
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Nicodemus says to them (being one of themselves),
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 Does our law judge a man before it have first heard from himself, and know what he does?
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 They answered and said to him, Art thou also of Galilee? Search and look, that no prophet arises out of Galilee.
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 And every one went to his home.
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

< John 7 >