< John 11 >
1 Now there was a certain [man] sick, Lazarus of Bethany, of the village of Mary and Martha her sister.
Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anadwala. Iye anali wa ku Betaniya, mudzi wa Mariya ndi mchemwali wake Marita.
2 It was [the] Mary who anointed the Lord with ointment and wiped his feet with her hair, whose brother Lazarus was sick.
Mariyayo ndi yemwe uja amene anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake. Lazaro wodwalayo anali mlongo wake.
3 The sisters therefore sent to him, saying, Lord, behold, he whom thou lovest is sick.
Choncho alongo ake anatumiza mawu kwa Yesu kuti, “Ambuye, uja amene Inu mumamukonda akudwala.”
4 But when Jesus heard [it], he said, This sickness is not unto death, but for the glory of God, that the Son of God may be glorified by it.
Atamva izi, Yesu anati, “Kudwalako safa nako. Koma akudwala kuti Mulungu alemekezedwe; ndi kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe chifukwa cha matendawo.”
5 Now Jesus loved Martha, and her sister, and Lazarus.
Yesu anakonda Marita, mchemwali wake ndi Lazaro.
6 When therefore he heard, He is sick, he remained two days then in the place where he was.
Koma atamva kuti Lazaro akudwala, Iye anakhalabe kumene anali masiku ena awiri.
7 Then after this he says to his disciples, Let us go into Judaea again.
Kenaka anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tibwerere ku Yudeya.”
8 The disciples say to him, Rabbi, [even but] now the Jews sought to stone thee, and goest thou thither again?
Ophunzira akewo anati, “Rabi, posachedwa pomwepa Ayuda anafuna kukugendani ndi miyala, koma Inu mukupitanso komweko?”
9 Jesus answered, Are there not twelve hours in the day? If any one walk in the day, he does not stumble, because he sees the light of this world;
Yesu anayankha kuti, “Kodi sipali maora khumi ndi awiri pa tsiku? Munthu amene amayenda masana sapunthwa, popeza akuona chifukwa cha kuwala kwa dziko lapansi.
10 but if any one walk in the night, he stumbles, because the light is not in him.
Koma amene akuyenda usiku amapunthwa, chifukwa kuwalako alibe.”
11 These things said he; and after this he says to them, Lazarus, our friend, is fallen asleep, but I go that I may awake him out of sleep.
Iye atatha kunena izi, anapitirira kuwawuza iwo kuti, “Bwenzi lathu Lazaro wagona tulo; koma Ine ndikupita kumeneko kukamudzutsa.”
12 The disciples therefore said to him, Lord, if he be fallen asleep, he will get well.
Ophunzira ake anayankha kuti, “Ambuye, ngati wagona adzapeza bwino.”
13 But Jesus spoke of his death, but they thought that he spoke of the rest of sleep.
Yesu ankayankhula za imfa yake koma ophunzira ake ankaganiza kuti amanena za tulo chabe.
14 Jesus therefore then said to them plainly, Lazarus has died.
Ndipo kenaka anawawuza momveka kuti, “Lazaro wamwalira.
15 And I rejoice on your account that I was not there, in order that ye may believe. But let us go to him.
Ine ndikukondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe kumeneko; koma kuti mukakhulupirire tiyeni tipiteko.”
16 Thomas therefore, called Didymus, said to his fellow disciples, Let us also go, that we may die with him.
Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, “Tiyeni nafenso tipite, kuti tikafere naye pamodzi.”
17 Jesus therefore [on] arriving found him to have been four days already in the tomb.
Yesu atafika, anapeza kuti Lazaro anali atagona mʼmanda masiku anayi.
18 Now Bethany was near Jerusalem, about fifteen stadia off,
Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pa mtunda wosachepera makilomita atatu,
19 and many of the Jews came to Martha and Mary, that they might console them concerning their brother.
ndipo Ayuda ambiri anabwera kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza pa imfa ya mʼbale wawo.
20 Martha then, when she heard Jesus is coming, went to meet him; but Mary sat in the house.
Pamene Marita anamva kuti Yesu akubwera, anapita kukakumana naye. Koma Mariya anatsala ku nyumba.
21 Martha therefore said to Jesus, Lord, if thou hadst been here, my brother had not died;
Marita anati kwa Yesu, “Ambuye, mukanakhala muli kuno, mlongo wanga sakanamwalira.
22 but even now I know, that whatsoever thou shalt ask of God, God will give thee.
Koma ine ndikudziwa kuti ngakhale tsopano Mulungu adzakupatsani chilichonse chimene mudzamupempha.”
23 Jesus says to her, Thy brother shall rise again.
Yesu anati kwa iye, “Mlongo wako adzauka.”
24 Martha says to him, I know that he will rise again in the resurrection in the last day.
Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”
25 Jesus said to her, I am the resurrection and the life: he that believes on me, though he have died, shall live;
Yesu anati kwa iye, “Ine ndine kuuka ndi moyo. Wokhulupirira Ine, angakhale amwalira adzakhala ndi moyo.
26 and every one who lives and believes on me shall never die. Believest thou this? (aiōn )
Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn )
27 She says to him, Yea, Lord; I believe that thou art the Christ, the Son of God, who should come into the world.
Marita anamuwuza Iye kuti, “Inde Ambuye, ine ndikukhulupirira kuti ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene abwera mʼdziko lapansi.”
28 And having said this, she went away and called her sister Mary secretly, saying, The teacher is come and calls thee.
Ndipo iye atanena izi anabwerera ndi kukayitana mchemwali wake Mariya namuyankhula monongʼona pambali, nati, “Aphunzitsi abwera ndipo akukuyitana.”
29 She, when she heard [that], rises up quickly and comes to him.
Mariya atamva izi, anayimirira mofulumira napita kwa Iye.
30 Now Jesus had not yet come into the village, but was in the place where Martha came to meet him.
Tsopano nʼkuti Yesu asanalowe mʼmudzi, koma anali akanali pa malo pamene Marita anakumana naye.
31 The Jews therefore who were with her in the house and consoling her, seeing Mary that she rose up quickly and went out, followed her, saying, She goes to the tomb, that she may weep there.
Ayuda amene ankamutonthoza Mariya mʼnyumba, anaona mmene iye anayimira mofulumira ndi kutuluka kunja, iwo anamutsata akuganizira kuti ankapita ku manda kukalirira kumeneko.
32 Mary therefore, when she came where Jesus was, seeing him, fell at his feet, saying to him, Lord, if thou hadst been here, my brother had not died.
Mariya anafika pamalo pamene panali Yesu ndipo atamuona, anagwa pa mapazi ake ndipo anati, “Ambuye mukanakhala muli kuno mlongo wanga sakanamwalira.”
33 Jesus therefore, when he saw her weeping, and the Jews who came with her weeping, was deeply moved in spirit, and was troubled,
Yesu ataona iye akulira, ndi Ayuda amene anabwera naye akuliranso, anakhudzidwa kwambiri ndi kuvutika mu mzimu.
34 and said, Where have ye put him? They say to him, Lord, come and see.
Iye anafunsa kuti, “Kodi mwamuyika kuti?” Iwo anayankha kuti, “Ambuye tiyeni mukaone.”
36 The Jews therefore said, Behold how he loved him!
Pamenepo Ayuda anati, “Taonani mmene Iye anamukondera Lazaro!”
37 And some of them said, Could not this [man], who has opened the eyes of the blind [man], have caused that this [man] also should not have died?
Koma ena a iwo anati, “Iye amatsekula maso a munthu wosaona, kodi sakanakhoza kuletsa kuti munthu uyu asamwalire?”
38 Jesus therefore, again deeply moved in himself, comes to the tomb. Now it was a cave, and a stone lay upon it.
Yesu atakhudzidwanso kwambiri anafika ku manda. Manda akewo anali phanga ndipo anatsekapo ndi mwala.
39 Jesus says, Take away the stone. Martha, the sister of the dead, says to him, Lord, he stinks already, for he is four days [there].
Yesu anati, “Chotsani mwala.” Marita mlongo wa womwalirayo anati, “Koma Ambuye, nthawi ino wayamba kununkha, pakuti wakhala mʼmenemu masiku anayi.”
40 Jesus says to her, Did I not say to thee, that if thou shouldest believe, thou shouldest see the glory of God?
Kenaka Yesu anati, “Kodi Ine sindinakuwuze kuti ngati iwe ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?”
41 They took therefore the stone away. And Jesus lifted up his eyes on high and said, Father, I thank thee that thou hast heard me;
Choncho iwo anachotsa mwalawo. Kenaka Yesu anayangʼana kumwamba ndikuti, “Atate, Ine ndikukuthokozani chifukwa mumandimvera.
42 but I knew that thou always hearest me; but on account of the crowd who stand around I have said [it], that they may believe that thou hast sent me.
Ine ndimadziwa kuti Inu mumandimvera nthawi zonse, koma Ine ndanena izi chifukwa cha anthu amene ayima pano, kuti iwo akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.”
43 And having said this, he cried with a loud voice, Lazarus, come forth.
Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!”
44 And the dead came forth, bound feet and hands with graveclothes, and his face was bound round with a handkerchief. Jesus says to them, Loose him and let him go.
Munthu womwalirayo anatuluka, womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za ku manda, ndi nkhope yake yokulungidwa nsalu. Yesu anawawuza kuti, “Mʼmasuleni, ndipo muloleni apite.”
45 Many therefore of the Jews who came to Mary and saw what he had done, believed on him;
Choncho Ayuda ambiri amene anabwera kudzamuchereza Mariya ndi kuona zimene Yesu anachita anamukhulupirira Iye.
46 but some of them went to the Pharisees and told them what Jesus had done.
Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi ndi kukawawuza zimene Yesu anachita.
47 The chief priests, therefore, and the Pharisees gathered a council, and said, What do we? for this man does many signs.
Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anayitanitsa msonkhano wa akulu olamulira. Iwo anafunsa kuti, “Kodi ife tikuchita chiyani? Pano pali munthu uyu akuchita zizindikiro zodabwitsa zambiri.
48 If we let him thus alone, all will believe on him, and the Romans will come and take away both our place and our nation.
Ngati ife timuleka kuti apitirize chotere, aliyense adzamukhulupirira Iye, ndipo kenaka Aroma adzabwera ndi kudzatenga malo athu pamodzi ndi dziko lathu.”
49 But a certain one of them, Caiaphas, being high priest that year, said to them, Ye know nothing
Kenaka mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chimenecho, anayankhula kuti, “Inu simukudziwa kanthu kalikonse!
50 nor consider that it is profitable for you that one man die for the people, and not that the whole nation perish.
Inu simukuzindikira kuti kuli bwino kwa inu kuti munthu mmodzi afe mʼmalo mwa anthu kusiyana ndi kuti mtundu wonse uwonongeke.”
51 But this he did not say of himself; but, being high priest that year, prophesied that Jesus was going to die for the nation;
Iye sananene izi mwa iye yekha, koma monga mkulu wa ansembe chaka chimenecho ananenera kuti Yesu anayanera kufera mtundu wa Ayuda,
52 and not for the nation only, but that he should also gather together into one the children of God who were scattered abroad.
ndipo osati mtundu okhawo komanso kwa ana ena a Mulungu onse obalalikana, kuti awabweretse pamodzi ndi kuwapanga kukhala amodzi.
53 From that day therefore they took counsel that they might kill him.
Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.
54 Jesus therefore walked no longer openly among the Jews, but went away thence into the country near the desert, to a city called Ephraim, and there he sojourned with the disciples.
Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.
55 But the passover of the Jews was near, and many went up to Jerusalem out of the country before the passover, that they might purify themselves.
Nthawi ya Paska wa Ayuda itayandikira, ambiri anakwera kupita ku Yerusalemu kuchokera ku madera a ku midzi chifukwa cha mwambo wa kuyeretsedwa Paska asanafike.
56 They sought therefore Jesus, and said among themselves, standing in the temple, What do ye think? that he will not come to the feast?
Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?”
57 Now the chief priests and the Pharisees had given commandment that if any one knew where he was, he should make it known, that they might take him.
Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.