< Job 36 >

1 And Elihu proceeded and said,
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Suffer me a little, and I will shew thee that I have yet words for God.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 I will fetch my knowledge from afar, and will ascribe righteousness to my Creator.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 For truly my words shall be no falsehood: one perfect in knowledge is with thee.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Lo, God is mighty, but despiseth not [any]; mighty in strength of understanding:
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 He saveth not the wicked alive; but he doeth justice to the afflicted.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 He withdraweth not his eyes from the righteous, but with kings on the throne doth he even set them for ever; and they are exalted.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 And if, bound in fetters, they be held in cords of affliction,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Then he sheweth them their work, and their transgressions, because they have increased.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 And he openeth their ear to discipline, and commandeth that they return from iniquity.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 If they hearken and serve [him], they shall accomplish their days in prosperity, and their years in pleasures.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 But if they hearken not, they shall pass away by the sword, and expire without knowledge.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 But the godless in heart heap up anger; they cry not when he bindeth them:
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Their soul dieth in youth, and their life is among the unclean.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 But he delivereth the afflicted in his affliction, and openeth their ear in [their] oppression.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Even so would he have allured thee out of the jaws of distress into a broad place, where there is no straitness; and the supply of thy table [would be] full of fatness.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 But thou art full of the judgments of the wicked: judgment and justice take hold [on thee].
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Because there is wrath, [beware] lest it take thee away through chastisement: then a great ransom could not avail thee.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Will he esteem thy riches? Not gold, nor all the resources of strength!
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Desire not the night, when peoples are cut off from their place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Take heed, turn not to iniquity; for this hast thou chosen rather than affliction.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Lo, God is exalted in his power: who teacheth as he?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Who hath appointed him his way? or who hath said, Thou hast wrought unrighteousness?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Remember that thou magnify his work, which men celebrate.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 All men look at it; man beholdeth [it] afar off.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Lo, God is great, and we comprehend [him] not, neither can the number of his years be searched out.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 For he draweth up the drops of water: they distil in rain from the vapour which he formeth,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Which the skies pour down [and] drop upon man abundantly.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 But can any understand the spreadings of the clouds, [or] the crashing of his pavilion?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Lo, he spreadeth his light around him, and covereth the bottom of the sea.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 For with them he judgeth the peoples; he giveth food in abundance.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 [His] hands he covereth with lightning, and commandeth it where it is to strike.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 His thundering declareth concerning him; the cattle even, concerning its coming.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >