< Job 31 >

1 I made a covenant with mine eyes; and how should I fix my regard upon a maid?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 For what would have been [my] portion of God from above, and what the heritage of the Almighty from on high?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Is not calamity for the unrighteous? and misfortune for the workers of iniquity?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Doth not he see my ways, and number all my steps?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 If I have walked with falsehood, and my foot hath hasted to deceit,
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 (Let me be weighed in an even balance, and God will take knowledge of my blamelessness; )
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 If my step have turned out of the way, and my heart followed mine eyes, and if any blot cleaveth to my hands;
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Let me sow, and another eat; and let mine offspring be rooted out.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 If my heart have been enticed unto a woman, so that I laid wait at my neighbour's door,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Let my wife grind for another, and let others bow down upon her.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 For this is an infamy; yea, it is an iniquity [to be judged by] the judges:
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 For it is a fire that consumeth to destruction, and would root out all mine increase.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 If I have despised the cause of my bondman or of my bondmaid, when they contended with me,
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 What then should I do when God riseth up? and if he visited, what should I answer him?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Did not he that made me in the womb make him? and did not One fashion us in the womb?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 If I have withheld the poor from [their] desire, or caused the eyes of the widow to fail;
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Or have eaten my morsel alone, so that the fatherless ate not thereof,
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 (For from my youth he grew up with me as with a father, and I have guided the [widow] from my mother's womb; )
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 If I have seen any perishing for want of clothing, or any needy without covering;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 If his loins have not blessed me, and if he were not warmed with the fleece of my lambs;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 If I have lifted up my hand against an orphan, because I saw my help in the gate:
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 [Then] let my shoulder fall from the shoulder-blade, and mine arm be broken from the bone!
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 For calamity from God was a terror to me, and by reason of his excellency I was powerless.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 If I have made gold my hope, or said to the fine gold, My confidence!
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 If I rejoiced because my wealth was great, and because my hand had gotten much;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 If I beheld the sun when it shone, or the moon walking in brightness,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 And my heart have been secretly enticed, so that my mouth kissed my hand:
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 This also would be an iniquity for the judge, for I should have denied the God who is above.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 If I rejoiced at the destruction of him that hated me, and exulted when evil befell him;
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 (Neither have I suffered my mouth to sin by asking his life with a curse; )
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 If the men of my tent said not, Who shall find one that hath not been satisfied with his meat? —
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 The stranger did not lodge without; I opened my doors to the pathway.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 If I covered my transgressions as Adam, by hiding mine iniquity in my bosom,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Because I feared the great multitude, and the contempt of families terrified me, so that I kept silence, and went not out of the door, ...
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Oh that I had one to hear me! Behold my signature: let the Almighty answer me! And let mine opponent write an accusation!
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Would I not take it upon my shoulder? I would bind it on to me [as] a crown;
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 I would declare unto him the number of my steps; as a prince would I come near to him.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 If my land cry out against me, and its furrows weep together;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 If I have eaten the fruits thereof without money, and have tormented to death the souls of its owners:
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Let thistles grow instead of wheat, and tares instead of barley. The words of Job are ended.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >