< Job 30 >

1 But now they that are younger than I have me in derision, whose fathers I would have disdained to set with the dogs of my flock.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Yea, whereto [should] the strength of their hands [profit] me, [men] in whom vigour hath perished?
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Withered up through want and hunger, they flee into waste places long since desolate and desert:
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 They gather the salt-wort among the bushes, and the roots of the broom for their food.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 They are driven forth from among [men] — they cry after them as after a thief —
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 To dwell in gloomy gorges, in caves of the earth and the rocks:
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 They bray among the bushes; under the brambles they are gathered together:
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Sons of fools, and sons of nameless sires, they are driven out of the land.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 And now I am their song, yea, I am their byword.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 They abhor me, they stand aloof from me, yea, they spare not to spit in my face.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 For he hath loosed my cord and afflicted me; so they cast off the bridle before me.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 At [my] right hand rise the young brood; they push away my feet, and raise up against me their pernicious ways;
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 They mar my path, they set forward my calamity, without any to help them;
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 They come in as through a wide breach: amid the confusion they roll themselves onward.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Terrors are turned against me; they pursue mine honour as the wind; and my welfare is passed away like a cloud.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 And now my soul is poured out in me; days of affliction have taken hold upon me.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 The night pierceth through my bones [and detacheth them] from me, and my gnawing pains take no rest:
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 By their great force they have become my raiment; they bind me about as the collar of my coat.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 He hath cast me into the mire, and I have become like dust and ashes.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 I cry unto thee, and thou answerest me not; I stand up, and thou lookest at me.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Thou art changed to a cruel one to me; with the strength of thy hand thou pursuest me.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Thou liftest me up to the wind; thou causest me to be borne away, and dissolvest my substance.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 For I know that thou wilt bring me to death, and into the house of assemblage for all living.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Indeed, no prayer [availeth] when he stretcheth out [his] hand: though they cry when he destroyeth.
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Did not I weep for him whose days were hard? was not my soul grieved for the needy?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 For I expected good, and there came evil; and I waited for light, but there came darkness.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 My bowels well up, and rest not; days of affliction have confronted me.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 I go about blackened, but not by the sun; I stand up, I cry in the congregation.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 I am become a brother to jackals, and a companion of ostriches.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 My skin is become black [and falleth] off me, and my bones are parched with heat.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 My harp also is [turned] to mourning, and my pipe into the voice of weepers.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Job 30 >