< Job 19 >

1 And Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 How long will ye vex my soul, and crush me with words?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 These ten times have ye reproached me; ye are not ashamed to stupefy me.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And be it [that] I have erred, mine error remaineth with myself.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 If indeed ye will magnify yourselves against me, and prove against me my reproach,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Know now that God hath overthrown me, and hath surrounded me with his net.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Behold, I cry out of wrong, and I am not heard; I cry aloud, but there is no judgment.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 He hath hedged up my way that I cannot pass, and he hath set darkness in my paths.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 He hath stripped me of my glory, and taken the crown from my head.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He breaketh me down on every side, and I am gone; and my hope hath he torn up as a tree.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 And he hath kindled his anger against me, and hath counted me unto him as one of his enemies.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 His troops have come together and cast up their way against me, and have encamped round about my tent.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 He hath put my brethren far from me, and mine acquaintance are quite estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 My kinsfolk have failed, and my known friends have forgotten me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 The sojourners in my house and my maids count me as a stranger; I am an alien in their sight.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 I called my servant, and he answered not; I entreated him with my mouth.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 My breath is strange to my wife, and my entreaties to the children of my [mother's] womb.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Even young children despise me; I rise up, and they speak against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 All my intimate friends abhor me, and they whom I loved are turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 My bones cleave to my skin and to my flesh, and I am escaped with the skin of my teeth.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Have pity upon me, have pity upon me, ye my friends; for the hand of God hath touched me.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Oh would that my words were written! oh that they were inscribed in a book!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 That with an iron style and lead they were graven in the rock for ever!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 And [as for] me, I know that my Redeemer liveth, and the Last, he shall stand upon the earth;
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And [if] after my skin this shall be destroyed, yet from out of my flesh shall I see God;
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Whom I shall see for myself, and mine eyes shall behold, and not another: — my reins are consumed within me.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 If ye say, How shall we persecute him? when the root of the matter is found in me,
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Be ye yourselves afraid of the sword! for the sword is fury against misdeeds, that ye may know there is a judgment.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >