< Job 1 >

1 There was a man in the land of Uz whose name was Job; and this man was perfect and upright, and one that feared God and abstained from evil.
Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
2 And there were born to him seven sons and three daughters.
Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
3 And his substance was seven thousand sheep, and three thousand camels, and five hundred yoke of oxen, and five hundred she-asses, and very many servants; and this man was greater than all the children of the east.
ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
4 And his sons went and made a feast in the house of each one on his day; and they sent and invited their three sisters to eat and to drink with them.
Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
5 And it was so, when the days of the feasting were gone about, that Job sent and hallowed them; and he rose up early in the morning, and offered up burnt-offerings [according to] the number of them all; for Job said, It may be that my children have sinned, and cursed God in their hearts. Thus did Job continually.
Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
6 And there was a day when the sons of God came to present themselves before Jehovah; and Satan came also among them.
Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
7 And Jehovah said to Satan, Whence comest thou? And Satan answered Jehovah and said, From going to and fro in the earth, and from walking up and down in it.
Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
8 And Jehovah said to Satan, Hast thou considered my servant Job, that there is none like him on the earth, a perfect and an upright man, one that feareth God and abstaineth from evil?
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
9 And Satan answered Jehovah and said, Doth Job fear God for nought?
Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
10 Hast not thou made a hedge about him, and about his house, and about all that he hath on every side? Thou hast blessed the work of his hands, and his substance is spread abroad in the land.
“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
11 But put forth thy hand now and touch all that he hath, [and see] if he will not curse thee to thy face!
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
12 And Jehovah said to Satan, Behold, all that he hath is in thy hand; only upon himself put not forth thy hand. So Satan went forth from the presence of Jehovah.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
13 And there was a day when his sons and his daughters were eating and drinking wine in the house of their brother, the firstborn.
Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
14 And there came a messenger to Job and said, The oxen were ploughing, and the asses feeding beside them;
wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
15 and [they of] Sheba fell [upon them] and took them, and the servants have they smitten with the edge of the sword; and I only am escaped, alone, to tell thee.
tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
16 While he was yet speaking, there came another and said, The fire of God fell from heaven and burned up the sheep and the servants, and consumed them; and I only am escaped, alone, to tell thee.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
17 While he was yet speaking, there came another and said, The Chaldeans made three bands, and fell upon the camels and took them, and the servants have they smitten with the edge of the sword; and I only am escaped, alone, to tell thee.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
18 While he was yet speaking, there came another and said, Thy sons and thy daughters were eating and drinking wine in the house of their brother, the firstborn;
Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
19 and behold, there came a great wind from over the wilderness, and smote the four corners of the house, and it fell upon the young men, and they died; and I only am escaped, alone, to tell thee.
mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
20 And Job rose up, and rent his mantle, and shaved his head, and fell down on the ground, and worshipped;
Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
21 and he said, Naked came I out of my mother's womb, and naked shall I return thither: Jehovah gave, and Jehovah hath taken away; blessed be the name of Jehovah!
nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
22 In all this Job sinned not, nor ascribed anything unseemly to God.
Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

< Job 1 >