< Hebrews 5 >
1 For every high priest taken from amongst men is established for men in things relating to God, that he may offer both gifts and sacrifices for sins;
Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuchokera pakati pa anthu ndipo amayikidwa kuti aziwayimirira pamaso pa Mulungu, kuti azipereka mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo.
2 being able to exercise forbearance towards the ignorant and erring, since he himself also is clothed with infirmity;
Popeza kuti iye mwini ali ndi zofowoka zake, amatha kuwalezera mtima amene ali osadziwa ndi osochera.
3 and, on account of this [infirmity], he ought, even as for the people, so also for himself, to offer for sins.
Chifukwa cha ichi, iye amadziperekera nsembe chifukwa cha machimo ake omwe ndiponso chifukwa cha machimo a anthu ena.
4 And no one takes the honour to himself but [as] called by God, even as Aaron also.
Palibe amene amadzipatsa yekha ulemu wotere, koma amachita kuyitanidwa ndi Mulungu monga momwe anayitanidwira Aaroni.
5 Thus the Christ also has not glorified himself to be made a high priest; but he who had said to him, Thou art my Son, I have to-day begotten thee.
Nʼchifukwa chake Khristu sanadzipatse yekha ulemu wokhala Mkulu wa ansembe. Koma Mulungu anamuwuza kuti, “Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.”
6 Even as also in another [place] he says, Thou [art] a priest for ever according to the order of Melchisedec. (aiōn )
Ndipo penanso anati, “Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya, monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
7 Who in the days of his flesh, having offered up both supplications and entreaties to him who was able to save him out of death, with strong crying and tears; (and having been heard because of his piety; )
Yesu, pa nthawi imene anali munthu pa dziko lapansi pano, anapereka mapemphero ake ndi zopempha mofuwula ndi misozi kwa Iye amene akanamupulumutsa ku imfa, ndipo anamumvera chifukwa anagonjera modzipereka.
8 though he were Son, he learned obedience from the things which he suffered;
Ngakhale Iye anali Mwana wa Mulungu anaphunzira kumvera pomva zowawa.
9 and having been perfected, became to all them that obey him, author of eternal salvation; (aiōnios )
Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. (aiōnios )
10 addressed by God [as] high priest according to the order of Melchisedec.
Ndipo Mulungu anamuyika kukhala Mkulu wa ansembe, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.
11 Concerning whom we have much to say, and hard to be interpreted in speaking [of it], since ye are become dull in hearing.
Tili ndi zambiri zoti tinganene pa zimenezi, koma ndi zovuta kukufotokozerani chifukwa ndinu ochedwa kuphunzira.
12 For when for the time ye ought to be teachers, ye have again need that [one] should teach you what [are] the elements of the beginning of the oracles of God, and are become such as have need of milk, [and] not of solid food.
Ngakhale kuti pa nthawi ino munayenera kukhala aphunzitsi, pakufunikabe munthu wina kuti abwerezenso kudzakuphunzitsani maphunziro oyambira a choonadi cha Mulungu. Ndinu ofunika mkaka osati chakudya cholimba!
13 For every one that partakes of milk [is] unskilled in the word of righteousness, for he is a babe;
Aliyense amene amangodya mkaka okha, akanali mwana wakhanda, sakudziwa bwino chiphunzitso cha chilungamo.
14 but solid food belongs to full-grown men, who, on account of habit, have their senses exercised for distinguishing both good and evil.
Koma chakudya cholimba ndi cha anthu okhwima msinkhu, amene pogwiritsa ntchito nzeru zawo, aphunzira kusiyanitsa chabwino ndi choyipa.