< Exodus 37 >

1 And Bezaleel made the ark of acacia-wood; two cubits and a half the length thereof, and a cubit and a half the breadth thereof, and a cubit and a half the height thereof.
Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
2 And he overlaid it with pure gold inside and outside, and made a border of gold upon it round about.
Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
3 And he cast for it four rings of gold, for its four corners: two rings on the one side of it, and two rings on the other side of it.
Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
4 And he made staves of acacia-wood and overlaid them with gold.
Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
5 And he put the staves into the rings on the sides of the ark, to carry the ark.
Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
6 — And he made a mercy-seat of pure gold; two cubits and a half the length thereof, and one cubit and a half the breadth thereof.
Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
7 And he made two cherubim of gold; of beaten work did he make them, at the two ends of the mercy-seat;
Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
8 one cherub at the end of one side, and one cherub at the end of the other side; out of the mercy-seat he made the two cherubim at the two ends thereof.
Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
9 And the cherubim spread out [their] wings over it, covering over with their wings the mercy-seat; and their faces were opposite to one another: the faces of the cherubim were [turned] toward the mercy-seat.
Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
10 And he made the table of acacia-wood; two cubits the length thereof, and a cubit the breadth thereof, and a cubit and a half the height thereof.
Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
11 And he overlaid it with pure gold, and made upon it a border of gold round about.
Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
12 And he made for it a margin of a hand-breadth round about; and made a border of gold for the margin thereof round about.
Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
13 And he cast for it four rings of gold, and put the rings on the four corners that were on the four feet thereof.
Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
14 Close to the margin were the rings, as receptacles of the staves to carry the table.
Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
15 And he made the staves of acacia-wood, and overlaid them with gold, to carry the table.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
16 And he made the utensils that were on the table, the dishes thereof, and the cups thereof, and the bowls thereof, and the goblets with which to pour out, of pure gold.
Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
17 And he made the candlestick of pure gold; [of] beaten work he made the candlestick: its base, and its shaft, its cups, its knobs, and its flowers were of itself.
Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
18 And six branches went out of the sides thereof — three branches of the candlestick out of the one side thereof, and three branches of the candlestick out of the other side thereof;
Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
19 [there were] three cups shaped like almonds in the one branch, a knob and a flower; and three cups shaped like almonds in the other branch, a knob and a flower: so in the six branches which went out of the candlestick.
Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
20 And in the candlestick were four cups, shaped like almonds, its knobs, and its flowers;
Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
21 and a knob under two branches thereof, and [again] a knob under two branches thereof, and [again] a knob under two branches thereof, for the six branches which went out of it.
Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
22 Their knobs and their branches were of itself — all of one beaten work of pure gold.
Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
23 And he made the seven lamps thereof, and the snuffers thereof, and the snuff-trays thereof, of pure gold.
Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
24 Of a talent of pure gold he made it, and all its utensils.
Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
25 And he made the altar of incense of acacia-wood; a cubit the length thereof, and a cubit the breadth thereof, square, and two cubits the height thereof: its horns were of itself.
Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
26 And he overlaid it with pure gold, the top thereof, and the sides thereof round about, and the horns thereof; and made upon it a border of gold round about.
Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
27 And he made two rings of gold for it under its border, by its two corners, on the two sides thereof, as receptacles for the staves with which to carry it.
Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
28 And he made the staves of acacia-wood, and overlaid them with gold.
Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
29 And he made the holy anointing oil, and the pure incense of fragrant drugs, according to the work of the perfumer.
Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

< Exodus 37 >