< Exodus 33 >

1 And Jehovah said to Moses, Depart, go up hence, thou and the people that thou hast brought up out of the land of Egypt, into the land that I swore unto Abraham, to Isaac, and to Jacob, saying, Unto thy seed will I give it,
Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
2 (and I will send an angel before thee, and dispossess the Canaanite, the Amorite, and the Hittite, and the Perizzite, the Hivite, and the Jebusite, )
Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
3 into a land flowing with milk and honey; for I will not go up in the midst of thee, for thou art a stiff-necked people, — lest I consume thee on the way.
Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
4 And when the people heard this evil word, they mourned; and no man put on his ornaments.
Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
5 Now Jehovah had said to Moses, Say unto the children of Israel, Ye are a stiff-necked people: in one moment I will come up into the midst of thee and will consume thee. And now put off thine ornaments from thee, and I will know what I will do unto thee.
Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
6 And the children of Israel stripped themselves of their ornaments at mount Horeb.
Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
7 And Moses took the tent, and pitched it outside the camp, far from the camp, and called it the Tent of meeting. And it came to pass [that] every one who sought Jehovah went out to the tent of meeting which was outside the camp.
Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
8 And it came to pass, when Moses went out to the tent, all the people rose up, and stood every man at the entrance of his tent, and they looked after Moses until he entered into the tent.
Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
9 And it came to pass when Moses entered into the tent, the pillar of cloud descended, and stood at the entrance of the tent, and [Jehovah] talked with Moses.
Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
10 And all the people saw the pillar of cloud standing at the entrance of the tent; and all the people rose and worshipped, every man at the entrance of his tent.
Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
11 And Jehovah spoke with Moses face to face, as a man speaks with his friend. And he returned to the camp; but his attendant, Joshua the son of Nun, a young man, departed not from within the tent.
Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
12 And Moses said to Jehovah, Behold, thou sayest unto me, Bring up this people; but thou dost not let me know whom thou wilt send with me; and thou hast said, I know thee by name, and thou hast also found grace in mine eyes.
Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
13 And now, if indeed I have found grace in thine eyes, make me now to know thy way, that I may know thee, that I may find grace in thine eyes; and consider that this nation is thy people!
Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
14 And he said, My presence shall go, and I will give thee rest.
Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
15 And he said to him, If thy presence do not go, bring us not up hence.
Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
16 And how shall it be known then that I have found grace in thine eyes — I and thy people? [Is it] not by thy going with us? so shall we be distinguished, I and thy people, from every people that is on the face of the earth.
Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
17 And Jehovah said to Moses, I will do this thing also that thou hast said; for thou hast found grace in mine eyes, and I know thee by name.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
18 And he said, Let me, I pray thee, see thy glory.
Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
19 And he said, I will make all my goodness pass before thy face, and I will proclaim the name of Jehovah before thee; and I will be gracious to whom I will be gracious, and I will shew mercy on whom I will shew mercy.
Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
20 And he said, Thou canst not see my face; for Man shall not see me, and live.
Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
21 And Jehovah said, Behold, [there is] a place by me: there shalt thou stand on the rock.
Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
22 And it shall come to pass, when my glory passeth by, that I will put thee in a cleft of the rock, and will cover thee with my hand, until I have passed by.
Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
23 And I will take away my hand, and thou shalt see me from behind; but my face shall not be seen.
Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”

< Exodus 33 >