< Exodus 26 >

1 And thou shalt make the tabernacle [with] ten curtains of twined byssus, and blue, and purple, and scarlet: with cherubim of artistic work shalt thou make them.
“Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
2 The length of one curtain shall be twenty-eight cubits, and the breadth of one curtain four cubits — one measure for all the curtains.
Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
3 Five of the curtains shall be coupled one to another, and [the other] five curtains coupled one to another.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
4 And thou shalt make loops of blue on the edge of the one curtain at the end of the coupling; and likewise shalt thou make [them] in the edge of the outermost curtain in the other coupling.
Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
5 Fifty loops shalt thou make in the one curtain, and fifty loops shalt thou make at the end of the curtain in the other coupling: the loops shall be opposite to one another.
Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
6 And thou shalt make fifty clasps of gold, and couple the curtains together with the clasps, that the tabernacle may be one [whole].
Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
7 And thou shalt make curtains of goats' [hair] for a tent over the tabernacle: eleven curtains shalt thou make them.
“Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
8 The length of one curtain shall be thirty cubits, and the breadth of one curtain four cubits — one measure for the eleven curtains.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
9 And thou shalt couple five of the curtains by themselves, and six of the curtains by themselves, and shalt double the sixth curtain in the front of the tent.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
10 And thou shalt make fifty loops on the edge of the outermost curtain of the coupling, and fifty loops on the edge of the curtain in the other coupling.
Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
11 And thou shalt make fifty clasps of copper, and put the clasps into the loops, and couple the tent, that it may be one [whole].
Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
12 And that which remaineth hanging over of the curtains of the tent, the half curtain that remaineth, shall hang over the rear of the tabernacle.
Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
13 And the cubit on the one side, and the cubit on the other side of that which remaineth in the length of the curtains of the tent, shall hang over the sides of the tabernacle on this side and on that side, to cover it.
Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
14 And thou shalt make a covering for the tent of rams' skins dyed red, and a covering of badgers' skins over [that].
Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
15 And the boards for the tabernacle thou shalt make of acacia-wood, standing up;
“Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
16 ten cubits the length of the board, and a cubit and a half the breadth of one board.
Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
17 One board shall have two tenons, connected one with the other: thus shalt thou make for all the boards of the tabernacle.
Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
18 And thou shalt make the boards for the tabernacle, twenty boards on the south side southward.
Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
19 And thou shalt make forty bases of silver under the twenty boards; two bases under one board for its two tenons, and two bases under another board for its two tenons.
Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
20 And for the other side of the tabernacle on the north side there shall be twenty boards.
Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
21 And their forty bases of silver; two bases under one board, and two bases under another board.
Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
22 And for the rear of the tabernacle westward thou shalt make six boards.
Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
23 And two boards shalt thou make for the corners of the tabernacle at the rear;
Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
24 and they shall be joined beneath, and together shall be united at the top thereof to one ring: thus shall it be for them both; they shall be for the two corners.
Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
25 And there shall be eight boards, and their bases, of silver, sixteen bases; two bases under one board, and two bases under another board.
Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
26 And thou shalt make bars of acacia-wood; five for the boards of the one side of the tabernacle,
“Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
27 and five bars for the boards of the other side of the tabernacle, and five bars for the boards of the side of the tabernacle at the rear westward;
mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
28 and the middle bar in the midst of the boards reaching from one end to the other.
Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
29 And thou shalt overlay the boards with gold, and make [of] gold their rings, the receptacles of the bars, and shalt overlay the bars with gold.
Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
30 And thou shalt set up the tabernacle according to its fashion, as hath been shewn thee on the mountain.
“Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
31 And thou shalt make a veil of blue, and purple, and scarlet, and twined byssus; of artistic work shall it be made, with cherubim.
“Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
32 And thou shalt attach it to four pillars of acacia-wood overlaid with gold, their hooks of gold; they shall be on four bases of silver.
Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
33 And thou shalt bring the veil under the clasps, and bring in thither, inside the veil, the ark of the testimony; and the curtain shall make a division to you between the holy [place] and the holiest of all.
Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
34 And thou shalt put the mercy-seat on the ark of the testimony in the holiest of all.
Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
35 And thou shalt set the table outside the veil, and the lamp-stand opposite to the table on the side of the tabernacle southward; and thou shalt put the table on the north side.
Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
36 And thou shalt make for the entrance of the tent a curtain of blue, and purple, and scarlet, and twined byssus, of embroidery.
“Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
37 And thou shalt make for the curtain five pillars of acacia[-wood], and overlay them with gold; their hooks shall be of gold; and thou shalt cast five bases of copper for them.
Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

< Exodus 26 >