< Colossians 3 >

1 If therefore ye have been raised with the Christ, seek the things [which are] above, where the Christ is, sitting at [the] right hand of God:
Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
2 have your mind on the things [that are] above, not on the things [that are] on the earth;
Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
3 for ye have died, and your life is hid with the Christ in God.
Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
4 When the Christ is manifested who [is] our life, then shall ye also be manifested with him in glory.
Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
5 Put to death therefore your members which [are] upon the earth, fornication, uncleanness, vile passions, evil lust, and unbridled desire, which is idolatry.
Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
6 On account of which things the wrath of God comes upon the sons of disobedience.
Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
7 In which ye also once walked when ye lived in these things.
Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
8 But now, put off, ye also, all [these] things, wrath, anger, malice, blasphemy, vile language out of your mouth.
Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
9 Do not lie to one another, having put off the old man with his deeds,
Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
10 and having put on the new, renewed into full knowledge according to [the] image of him that has created him;
ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
11 wherein there is not Greek and Jew, circumcision and uncircumcision, barbarian, Scythian, bondman, freeman; but Christ [is] everything, and in all.
Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
12 Put on therefore, as [the] elect of God, holy and beloved, bowels of compassion, kindness, lowliness, meekness, longsuffering;
Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
13 forbearing one another, and forgiving one another, if any should have a complaint against any; even as the Christ has forgiven you, so also [do] ye.
Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
14 And to all these [add] love, which is the bond of perfectness.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
15 And let the peace of Christ preside in your hearts, to which also ye have been called in one body, and be thankful.
Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
16 Let the word of the Christ dwell in you richly, in all wisdom teaching and admonishing one another, in psalms, hymns, spiritual songs, singing with grace in your hearts to God.
Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
17 And everything, whatever ye may do in word or in deed, [do] all things in [the] name of [the] Lord Jesus, giving thanks to God the Father by him.
Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
18 Wives, be subject to [your] husbands, as is fitting in [the] Lord.
Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Husbands, love your wives, and be not bitter against them.
Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Children, obey your parents in all things, for this is well-pleasing in [the] Lord.
Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Fathers, do not vex your children, to the end that they be not disheartened.
Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Bondmen, obey in all things your masters according to flesh; not with eye-services, as men-pleasers, but in simplicity of heart, fearing the Lord.
Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
23 Whatsoever ye do, labour at it heartily, as [doing it] to the Lord, and not to men;
Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
24 knowing that of [the] Lord ye shall receive the recompense of the inheritance; ye serve the Lord Christ.
Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
25 For he that does a wrong shall receive the wrong he has done, and there is no respect of persons.
Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

< Colossians 3 >