< 2 Samuel 3 >

1 And the war was long between the house of Saul and the house of David; but David became continually stronger, and the house of Saul became continually weaker.
Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
2 And to David were sons born in Hebron: his firstborn was Amnon, of Ahinoam the Jizreelitess;
Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
3 and his second, Chileab, of Abigail the wife of Nabal the Carmelite; and the third, Absalom the son of Maachah, daughter of Talmai king of Geshur;
Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
4 and the fourth, Adonijah the son of Haggith; and the fifth, Shephatiah the son of Abital;
wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
5 and the sixth, Ithream, of Eglah David's wife. These were born to David in Hebron.
ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
6 And it came to pass while there was war between the house of Saul and the house of David, that Abner made himself strong for the house of Saul.
Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
7 And Saul had a concubine whose name was Rizpah, the daughter of Aiah. And [Ishbosheth] said to Abner, Why hast thou gone in to my father's concubine?
Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
8 Then was Abner very wroth for the words of Ishbosheth, and said, Am I a dog's head, I who against Judah do shew kindness this day to the house of Saul thy father, to his brethren, and to his friends, and have not delivered thee into the hand of David, that thou reproachest me this day with the fault of this woman?
Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
9 So do God to Abner, and more also, if, as Jehovah has sworn to David, I do not so to him;
Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
10 to translate the kingdom from the house of Saul, and to set up the throne of David over Israel and over Judah, from Dan even to Beer-sheba!
Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
11 And he could not answer Abner a word again, because he feared him.
Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
12 And Abner sent messengers to David on his behalf, saying, Whose is the land? saying [also], Make thy covenant with me, and behold, my hand shall be with thee, to turn all Israel to thee.
Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
13 And he said, Well, I will make a covenant with thee; only I require one thing of thee, that is, Thou shalt not see my face, except thou first bring Michal Saul's daughter, when thou comest to see my face.
Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
14 And David sent messengers to Ishbosheth Saul's son, saying, Deliver me my wife Michal, whom I espoused to me for a hundred foreskins of the Philistines.
Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
15 And Ishbosheth sent, and took her from [her] husband, from Phaltiel the son of Laish.
Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
16 And her husband went with her along weeping behind her to Bahurim. Then said Abner to him, Go, return. And he returned.
Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
17 Now Abner had communicated with the elders of Israel, saying, Ye sought for David aforetime to be king over you;
Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
18 and now do [it], for Jehovah has spoken of David, saying, By my servant David will I save my people Israel out of the hand of the Philistines, and out of the hand of all their enemies.
Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
19 And Abner also spoke in the ears of Benjamin; and Abner went also to speak in the ears of David in Hebron all that seemed good to Israel, and that seemed good to the whole house of Benjamin.
Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
20 So Abner came to David to Hebron, and twenty men with him. And David made Abner and the men that were with him a repast.
Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
21 And Abner said to David, I will arise and go, and will gather all Israel to my lord the king, that they may make a covenant with thee, and that thou mayest reign over all that thy heart desires. And David sent Abner away; and he went in peace.
Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
22 And behold, the servants of David and Joab came from an expedition, and brought in a great spoil with them; but Abner was no longer with David in Hebron, for he had sent him away, and he had gone in peace.
Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
23 And Joab and all the host that was with him came; and they told Joab, saying, Abner the son of Ner came to the king, and he has sent him away; and he is gone in peace.
Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
24 Then Joab came to the king, and said, What hast thou done? behold, Abner came to thee; why is it [that] thou hast sent him away, and he is gone?
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
25 Thou knowest Abner the son of Ner, that he came to deceive thee, to know thy going out and thy coming in, and to know all that thou doest.
Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
26 And when Joab was come out from David, he sent messengers after Abner, who brought him again from the well of Sirah; but David did not know it.
Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
27 And when Abner was returned to Hebron, Joab took him aside in the gate to speak with him secretly, and smote him there in the belly, that he died, for the blood of Asahel his brother.
Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
28 And afterwards David heard [it], and he said, I and my kingdom are guiltless before Jehovah for ever from the blood of Abner the son of Ner:
Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
29 let it fall on the head of Joab, and on all his father's house; and let there not fail from the house of Joab one that has an issue, or that is a leper, or that leans on a staff, or that falls by the sword, or that lacks bread!
Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
30 So Joab and Abishai his brother killed Abner, because he had slain their brother Asahel at Gibeon in the battle.
(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
31 And David said to Joab, and to all the people that were with him, Rend your garments, and gird yourselves with sackcloth, and mourn before Abner. And king David followed the bier.
Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
32 And they buried Abner in Hebron; and the king lifted up his voice and wept at the grave of Abner; and all the people wept.
Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
33 And the king lamented over Abner, and said, Should Abner die as a fool dieth?
Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34 Thy hands were not bound, Nor thy feet put into fetters; As a man falleth before wicked men, Fellest thou! And all the people wept again over him.
Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
35 And all the people came to cause David to eat bread while it was yet day; but David swore, saying, So do God to me, and more also, if I taste bread or aught else till the sun be down!
Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
36 And all the people remarked it, and it pleased them; as whatever the king did pleased all the people.
Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
37 And all the people and all Israel understood that day that it was not of the king to put Abner the son of Ner to death.
Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
38 And the king said to his servants, Know ye not that there is a prince and a great man fallen this day in Israel?
Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
39 And I am this day weak, though anointed king; and these men, the sons of Zeruiah, are too hard for me: Jehovah reward the doer of evil according to his wickedness!
Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

< 2 Samuel 3 >