< 2 Samuel 17 >

1 And Ahithophel said to Absalom, Let me, I pray, choose out twelve thousand men, and I will arise and pursue after David to-night;
Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
2 and I will come upon him while he is weary and weak-handed, and will make him afraid; and all the people that are with him shall flee; and I will smite the king only;
Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
3 and I will bring back all the people to thee. The man whom thou seekest is as if all returned: all the people shall be in peace.
ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
4 And the saying was right in the eyes of Absalom, and in the eyes of all the elders of Israel.
Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
5 And Absalom said, Call now Hushai the Archite also, and we will hear also what he says.
Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
6 And Hushai came to Absalom, and Absalom spoke to him saying, Ahithophel has spoken after this manner: shall we carry out his word? If not, speak thou.
Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
7 And Hushai said to Absalom, The counsel that Ahithophel has given this time is not good.
Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
8 And Hushai said, Thou knowest thy father and his men, that they are mighty men, and they are of exasperated spirit, as a bear robbed of her whelps in the field; and thy father is a man of war, and will not lodge with the people.
Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
9 Behold, he is hid now in some pit, or some such place; and it will come to pass, when some of them fall at the first, whoever heareth it will say, There has been slaughter among the people that follow Absalom,
Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
10 and even the valiant man whose heart is as the heart of a lion shall utterly melt; for all Israel knows that thy father is a mighty man, and they that are with him are valiant men.
Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
11 But I counsel that all Israel be speedily gathered to thee, from Dan even to Beer-sheba, as the sand that is by the sea for multitude; and that thou go to battle in thine own person.
“Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
12 And we shall come upon him in some place where he shall be found, and we will light upon him as the dew falls on the ground; and of him and of all the men that are with him there shall not be left so much as one.
Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
13 And if he withdraw into a city, then shall all Israel bring ropes to that city, and we will draw it into the torrent, until there be not one small stone found there.
Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
14 And Absalom and all the men of Israel said, The counsel of Hushai the Archite is better than the counsel of Ahithophel. And Jehovah had appointed to defeat the good counsel of Ahithophel, in order that Jehovah might bring evil upon Absalom.
Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
15 And Hushai said to Zadok and to Abiathar the priests, Thus and thus did Ahithophel counsel Absalom and the elders of Israel; and thus and thus have I counselled.
Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
16 And now send quickly, and tell David saying, Lodge not this night in the plains of the wilderness, but speedily pass over; lest the king be swallowed up, and all the people that are with him.
Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
17 And Jonathan and Ahimaaz stayed by En-rogel; and the maid went and told them; and they went and told king David, for they might not be seen to come into the city.
Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
18 But a lad saw them, and told Absalom. Then they went both of them away quickly, and came to the house of a man at Bahurim, who had a well in his court; and they went down there.
Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
19 And the woman took and spread the covering over the well's mouth, and spread ground corn on it; and the thing was not known.
Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
20 And Absalom's servants came to the woman to the house, and said, Where are Ahimaaz and Jonathan? And the woman said to them, They have gone over the brook of water. And they sought and could not find [them], and returned to Jerusalem.
Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
21 And it came to pass after they had departed, that they came up out of the well, and went and told king David; and they said to David, Arise and pass quickly over the water; for thus has Ahithophel counselled against you.
Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
22 Then David arose, and all the people that were with him, and they passed over the Jordan; by the morning light there was not one of them missing that had not gone over the Jordan.
Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
23 And when Ahithophel saw that his counsel was not followed, he saddled his ass, and arose and went to his house, to his city, and gave charge to his household, and hanged himself, and he died; and he was buried in the sepulchre of his father.
Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
24 And David came to Mahanaim. And Absalom passed over the Jordan, he and all the men of Israel with him.
Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
25 And Absalom set Amasa over the host instead of Joab; which Amasa was the son of a man whose name was Jithra the Israelite, that went in to Abigail the daughter of Nahash, sister to Zeruiah, Joab's mother.
Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
26 And Israel and Absalom encamped in the land of Gilead.
Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
27 And as soon as David came to Mahanaim, Shobi the son of Nahash of Rabbah of the children of Ammon, and Machir the son of Ammiel of Lo-debar, and Barzillai the Gileadite of Rogelim,
Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
28 brought beds, and basons, and earthen vessels, and wheat, and barley, and flour, and parched [corn], and beans, and lentils, and parched [pulse],
anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
29 and honey, and cream, and sheep, and cheese of kine to David, and to the people that were with him, to eat; for they said, The people is hungry, and weary, and thirsty in the wilderness.
uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”

< 2 Samuel 17 >