< 1 John 1 >

1 That which was from [the] beginning, that which we have heard, which we have seen with our eyes; that which we contemplated, and our hands handled, concerning the word of life;
Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
2 (and the life has been manifested, and we have seen, and bear witness, and report to you the eternal life, which was with the Father, and has been manifested to us: ) (aiōnios g166)
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios g166)
3 that which we have seen and heard we report to you, that ye also may have fellowship with us; and our fellowship [is] indeed with the Father, and with his Son Jesus Christ.
Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
4 And these things write we to you that your joy may be full.
Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
5 And this is the message which we have heard from him, and declare to you, that God is light, and in him is no darkness at all.
Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
6 If we say that we have fellowship with him, and walk in darkness, we lie, and do not practise the truth.
Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
7 But if we walk in the light as he is in the light, we have fellowship with one another, and the blood of Jesus Christ his Son cleanses us from all sin.
Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
8 If we say that we have no sin, we deceive ourselves, and the truth is not in us.
Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
9 If we confess our sins, he is faithful and righteous to forgive us [our] sins, and cleanse us from all unrighteousness.
Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
10 If we say that we have not sinned, we make him a liar, and his word is not in us.
Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.

< 1 John 1 >