< 1 Chronicles 24 >

1 And the divisions of the sons of Aaron: the sons of Aaron, Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 And Nadab and Abihu died before their father, and had no children; and Eleazar and Ithamar exercised the priesthood.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 And David distributed them, both Zadok of the sons of Eleazar, and Ahimelech of the sons of Ithamar, according to their office in their service.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 And there were more head-men found of the sons of Eleazar than of the sons of Ithamar, and [thus] were they divided: of the sons of Eleazar there were sixteen heads of fathers' houses, and eight of the sons of Ithamar according to their fathers' houses.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 And they were divided by lot, one with another; for the princes of the sanctuary and the princes of God were of the sons of Eleazar and of the sons of Ithamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 And Shemaiah the son of Nethaneel the scribe, [one] of the Levites, inscribed them before the king, and the princes, and Zadok the priest, and Ahimelech the son of Abiathar, and the chief fathers of the priests and Levites: one father's house was drawn for Eleazar, and one drawn for Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 And the first lot came forth for Jehoiarib, the second for Jedaiah,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 the third for Harim, the fourth for Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 the fifth for Malchijah, the sixth for Mijamin,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 the seventh for Hakkoz, the eighth for Abijah,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 the ninth for Jeshuah, the tenth for Shecaniah,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 the eleventh for Eliashib, the twelfth for Jakim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 the thirteenth for Huppah, the fourteenth for Jeshebeab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 the fifteenth for Bilgah, the sixteenth for Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 the seventeenth for Hezir, the eighteenth for Happizez,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 the nineteenth for Pethahiah, the twentieth for Ezekiel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 the twenty-first for Jachin, the twenty-second for Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 the twenty-third for Delaiah, the twenty-fourth for Maaziah.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 This is their ordering in their service to come into the house of Jehovah, according to their ordinance, through Aaron their father, as Jehovah the God of Israel had commanded him.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 And as for the rest of the sons of Levi: of the sons of Amram, Shubael; of the sons of Shubael, Jehdeiah.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Of Rehabiah, of the sons of Rehabiah, the head was Jishijah.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Of the Jizharites, Shelomoth; of the sons of Shelomoth, Jahath.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 — And the sons [of Hebron]: Jerijah [the head], Amariah the second, Jahaziel the third, Jekameam the fourth.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 The sons of Uzziel, Micah; of the sons of Micah, Shamir;
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 the brother of Micah was Jishijah; of the sons of Jishijah, Zechariah.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 The sons of Merari: Mahli and Mushi; the sons of Jaaziah, his son.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 The sons of Merari by Jaaziah his son: Shoham, and Zaccur, and Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Of Mahli: Eleazar, who had no sons.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Of Kish, the sons of Kish: Jerahmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 And the sons of Mushi: Mahli, and Eder, and Jerimoth. These were the sons of the Levites according to their fathers' houses.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 These likewise cast lots just as their brethren the sons of Aaron before David the king, and Zadok, and Ahimelech, and the chief fathers of the priests and Levites, — the chief fathers just as the youngest of their brethren.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronicles 24 >