< 1 Chronicles 12 >

1 Now these are they that came to David to Ziklag, while he kept still close because of Saul the son of Kish; and they were among the mighty men who helped him in the conflict;
Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
2 armed with bows, using both the right hand and the left with stones and with arrows on the bow; [they were] of Saul's brethren of Benjamin:
Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
3 the chief Ahiezer, and Joash, the sons of Shemaah the Gibeathite; and Jeziel, and Pelet, the sons of Azmaveth; and Berachah, and Jehu the Anathothite,
Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
4 and Jishmaiah the Gibeonite, a mighty man among the thirty, and over the thirty; and Jeremiah, and Jahaziel, and Johanan, and Jozabad the Gederathite.
ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
5 Eluzai, and Jerimoth, and Bealiah, and Shemariah, and Shephatiah the Haruphite;
Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
6 Elkanah, and Jishijah, and Azareel, and Joezer, and Jashobeam, the Korahites;
Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
7 and Joelah, and Zebadiah, the sons of Jeroham of Gedor.
ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
8 And of the Gadites, there separated themselves to David in the stronghold in the wilderness mighty men of valour, men fit for the service of war, armed with shield and spear; whose faces were [like] the faces of lions, and who were swift as the gazelles upon the mountains:
Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
9 Ezer the first, Obadiah the second, Eliab the third,
Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
10 Mishmannah the fourth, Jeremiah the fifth,
wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
11 Attai the sixth, Eliel the seventh,
wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
12 Johanan the eighth, Elzabad the ninth,
wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
13 Jeremiah the tenth, Machbannai the eleventh.
wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
14 These were of the sons of Gad, captains of the host: one of the least was over a hundred, and the greatest over a thousand.
Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
15 These are they that went over Jordan in the first month, when it overflows all its banks, and they put to flight all [them] of the valleys, toward the east and toward the west.
Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
16 And there came of the children of Benjamin and Judah to the stronghold to David.
Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
17 And David went out to meet them, and answered and said to them, If ye come peaceably to me to help me, my heart shall be knit unto you; but if to betray me to mine enemies, seeing there is no wrong in my hands, the God of our fathers see [it] and rebuke [it].
Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
18 And the Spirit came upon Amasai, the chief of the captains, [and he said, ] Thine [are we], David, And with thee, thou son of Jesse: Peace, peace be to thee! And peace be to thy helpers! For thy God helps thee. And David received them, and made them chiefs of bands.
Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
19 And there fell some of Manasseh to David, when he came with the Philistines against Saul to battle: but they helped them not; for the lords of the Philistines upon deliberation sent him away, saying, He will fall to his master Saul at the peril of our heads.
Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
20 As he went away to Ziklag, there fell to him of Manasseh: Adnah, and Jozabad, and Jediael, and Michael, and Jozabad, and Elihu, and Zilthai, captains of the thousands that were of Manasseh.
Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
21 And they helped David in his expeditions; for they were all mighty men of valour, and were captains in the host.
Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
22 For day by day there came [men] to David to help him, until it was a great camp, like the camp of God.
Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
23 And this is the number of the men equipped for military service, who came to David to Hebron, to transfer the kingdom of Saul to him, according to the word of Jehovah.
Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
24 The children of Judah that bore shield and spear were six thousand eight hundred, equipped for military service.
Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
25 Of the children of Simeon, mighty men of valour for war, seven thousand one hundred.
Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
26 Of the children of Levi four thousand six hundred.
Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
27 And Jehoiada the prince of Aaron, and with him were three thousand seven hundred;
mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
28 and Zadok, a valiant young man, and his father's house two and twenty chief men.
ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
29 And of the children of Benjamin, the brethren of Saul, three thousand; but hitherto the greater part of them had adhered to the house of Saul.
Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
30 And of the children of Ephraim twenty thousand eight hundred, mighty men of valour, men of name in their fathers' houses.
Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
31 And of the half tribe of Manasseh eighteen thousand, who were expressed by name, to come and make David king.
Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
32 And of the children of Issachar, who had understanding of the times, to know what Israel ought to do, the heads of them were two hundred; and all their brethren were at their bidding.
Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
33 Of Zebulun, such as went forth in the host, armed for war with all weapons of war, fifty thousand, keeping rank without double heart.
Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
34 And of Naphtali a thousand captains, and with them thirty-seven thousand with shield and spear.
Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
35 And of the Danites armed for war twenty-eight thousand six hundred.
Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
36 And of Asher such as went forth in the host, to set themselves in battle array, forty thousand.
Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
37 And from the other side of the Jordan, of the Reubenites, and the Gadites, and of the half tribe of Manasseh, with all manner of weapons of war for battle, a hundred and twenty thousand.
Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
38 All of them men of war, keeping rank in battle array, came with a perfect heart to Hebron, to make David king over all Israel; and all the rest also of Israel were of one heart to make David king.
Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
39 And there they were with David three days, eating and drinking; for their brethren had prepared for them;
Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
40 and those too that were near them, as far as Issachar and Zebulun and Naphtali, brought food on asses, and on camels, and on mules, and on oxen; provisions of meal, fig-cakes and raisin-cakes, and wine and oil, and oxen and sheep, abundantly; for there was joy in Israel.
Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

< 1 Chronicles 12 >