< Zechariah 14 >

1 Behold, the days of the Lord will arrive, and your spoils will be divided in your midst.
Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
2 And I will gather all the Gentiles in battle against Jerusalem, and the city will be captured, and the houses will be ravaged, and the women will be violated. And the central part of the city will go forth into captivity, and the remainder of the people will not be taken away from the city.
Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
3 Then the Lord will go forth, and he will fight against those Gentiles, just as when he fought in the day of conflict.
Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
4 And his feet will stand firm, in that day, upon the Mount of Olives, which is opposite Jerusalem towards the East. And the mount of Olives will be divided down its center part, towards the East and towards the West, with a very great rupture, and the center of the mountain will be separated towards the North, and its center towards the Meridian.
Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
5 And you will flee to the valley of those mountains, because the valley of the mountains will be joined all the way to the next. And you will flee, just as you fled from the face of the earthquake in the days of Uzziah king of Judah. And the Lord my God will arrive, and all the saints with him.
Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
6 And this shall be in that day: there will not be light, only cold and frost.
Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
7 And there will be one day, which is known to the Lord, not day and not night. And in the time of the evening, there will be light.
Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
8 And this shall be in that day: the living waters will go out from Jerusalem, half of them towards the East sea, and half of them towards the furthest sea. They will be in summer and in winter.
Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
9 And the Lord will be King over all the earth. In that day, there will be one Lord, and his name will be one.
Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
10 And all the land will return even to the desert, from the hill of Rimmon to the South of Jerusalem. And she will be exalted, and she will dwell in her own place, from the gate of Benjamin even to the place of the former gate, and even to the gate of the corners, and from the tower of Hananel even to the pressing room of the king.
Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
11 And they will dwell in it, and there will be no further anathema, but Jerusalem shall sit securely.
Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
12 And this will be the plague by which the Lord will strike all the Gentiles that have fought against Jerusalem. The flesh of each one will waste away while they are standing on their feet, and their eyes will be consumed in their sockets, and their tongue will be consumed in their mouth.
Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
13 In that day, there will be a great tumult from the Lord among them. And a man will take the hand of his neighbor, and his hand will be clasped upon the hand of his neighbor.
Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
14 And even Judah will fight against Jerusalem. And the riches of all the Gentiles will be gathered together around them: gold, and silver, and more than enough garments.
Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
15 And, like the ruin of the horse, and the mule, and the camel, and the donkey, and all the beasts of burden, which will have been in those encampments, so will be this ruination.
Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
16 And all those who will be the remnant of all the Gentiles that came against Jerusalem, will go up, from year to year, to adore the King, the Lord of hosts, and to celebrate the feast of tabernacles.
Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
17 And this shall be: whoever will not go up, from the families of the earth to Jerusalem, so as to adore the King, the Lord of hosts, there will be no showers upon them.
Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
18 But if even the family of Egypt will go not up, nor approach, neither will it be upon them, but there will be ruin, by which the Lord will strike all the Gentiles, who will not go up to celebrate the feast of tabernacles.
Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
19 This will be the sin of Egypt, and this will be the sin of all the Gentiles, who will not go up to celebrate the feast of tabernacles.
Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
20 In that day, that which is on the bridle of the horse will be holy to the Lord. And even the cooking pots in the house of the Lord will be like holy vessels before the altar.
Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
21 And every cooking pot in Jerusalem and Judah will be sanctified to the Lord of hosts. And all those who make sacrifices will come and take from them, and will cook with them. And the merchant will no longer be in the house of the Lord of hosts, in that day.
Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.

< Zechariah 14 >