< Psalms 62 >

1 Unto the end. For Jeduthun. A Psalm of David. Will my soul not be subject to God? For from him is my salvation.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
2 Yes, he himself is my God and my salvation. He is my supporter; I will be moved no more.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
3 How is it that you rush against a man? Every one of you puts to death, as if you were pulling down a ruined wall, leaning over and falling apart.
Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
4 So, truly, they intended to reject my price. I ran in thirst. They blessed with their mouth and cursed with their heart.
Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
5 Yet, truly, my soul will be subject to God. For from him is my patience.
Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
6 For he is my God and my Savior. He is my helper; I will not be expelled.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
7 In God is my salvation and my glory. He is the God of my help, and my hope is in God.
Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
8 All peoples gathered together: trust in him. Pour out your hearts in his sight. God is our helper for eternity.
Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
9 So, truly, the sons of men are untrustworthy. The sons of men are liars in the scales, so that, by emptiness, they may deceive among themselves.
Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Do not trust in iniquity, and do not desire plunder. If riches flow toward you, do not be willing to set your heart on them.
Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
11 God has spoken once. I have heard two things: that power belongs to God,
Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12 and that mercy belongs to you, O Lord. For you will repay each one according to his works.
komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.

< Psalms 62 >