< Psalms 60 >

1 Unto the end. For those who will be changed, with the inscription of a title, of David himself, for instruction: when he set fire to Mesopotamia of Syria and Sobal, and Joab turned back and struck Idumea, in the valley of the salt pits, twelve thousand men. O God, you have rejected us, and you have ruined us. You became angry, and yet you have been merciful to us.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 You have moved the earth, and you have disturbed it. Heal its breaches, for it has been moved.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 You have revealed to your people difficulties. You have made us drink the wine of remorse.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 You have given a warning sign to those who fear you, so that they may flee from before the face of the bow, so that your beloved may be delivered.
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Save me with your right hand, and hear me.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God has spoken in his holy place: I will rejoice, and I will divide Shechem, and I will measure the steep valley of the tabernacles.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Gilead is mine, and Manasseh is mine. And Ephraim is the strength of my head. Judah is my king.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab is the cooking pot of my hope. Into Idumea, I will extend my shoe. To me, the foreigners have been made subject.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Who will lead me into the fortified city? Who will lead me all the way to Idumea?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Will not you, O God, who has rejected us? And will not you, O God, go out with our armies?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Grant us help from tribulation. For salvation from man is empty.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 In God, we will act virtuously. And those who trouble us, he will lead to nothing.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psalms 60 >