< Psalms 39 >
1 Unto the end. For Jeduthun himself. A Canticle of David. I said, “I will keep to my ways, so that I will not offend with my tongue.” I posted a guard at my mouth, when a sinner took up a position against me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 I was silenced and humbled, and I was quiet before good things, and my sorrow was renewed.
Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
3 My heart grew hot within me, and, during my (meditation) a fire would flare up.
Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 I spoke with my tongue, “O Lord, make me know my end, and what the number of my days will be, so that I may know what is lacking to me.”
“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Behold, you have made my days measurable, and, before you, my substance is as nothing. Yet truly, all things are vanity: every living man.
Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
6 So then, truly man passes by like an image; even so, he is disquieted in vain. He stores up, and he knows not for whom he will gather these things.
Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 And now, what is it that awaits me? Is it not the Lord? And my substance is with you.
“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Rescue me from all my iniquities. You have handed me over as a reproach to the foolish.
Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 I was silenced, and I did not open my mouth, because it was you who acted.
Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Remove your scourges from me.
Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 I fall short at corrections from the strength of your hand. For you have chastised man for iniquity. And you have made his soul shrink away like a spider. Nevertheless, it is in vain that any man be disquieted.
Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
12 O Lord, heed my prayer and my supplication. Pay attention to my tears. Do not be silent. For I am a newcomer with you, and a sojourner, just as all my fathers were.
“Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
13 Forgive me, so that I may be refreshed, before I will go forth and be no more.
Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”