< Psalms 146 >

1 Alleluia. Of Haggai and Zachariah.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Praise the Lord, O my soul. I will praise the Lord with my life. I will sing psalms to my God as long as I shall be. Do not trust in the leaders,
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 in the sons of men, in whom there is no salvation.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 His spirit will depart, and he will return to his earth. In that day, all their thoughts will perish.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Blessed is he whose help is the God of Jacob: his hope is in the Lord God himself,
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 who made heaven and earth, the sea, and all the things that are in them.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 He preserves the truth forever. He executes judgment for those who suffer injury. He provides food for the hungry. The Lord releases those who are bound.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 The Lord enlightens the blind. The Lord sets upright those who have been thrown down. The Lord loves the just.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 The Lord watches over new arrivals. He will support the orphan and the widow. And he will destroy the ways of sinners.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 The Lord shall reign forever: your God, O Zion, from generation to generation.
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psalms 146 >