< Psalms 116 >

1 Alleluia. I have loved: therefore, the Lord will heed the voice of my prayer.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 For he has inclined his ear to me. And in my days, I will call upon him.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 The sorrows of death have surrounded me, and the perils of Hell have found me. I have found tribulation and sorrow. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 And so, I called upon the name of the Lord. O Lord, free my soul.
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Merciful is the Lord, and just. And our God is compassionate.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 The Lord is the keeper of little ones. I was humbled, and he freed me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Turn again, my soul, to your rest. For the Lord has done good to you.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For he has rescued my soul from death, my eyes from tears, my feet from slipping.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I will please the Lord in the land of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Alleluia. I had confidence, because of what I was saying, but then I was greatly humbled.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I said in my excess, “Every man is a liar.”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 What shall I repay to the Lord, for all the things that he has repaid to me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will take up the cup of salvation, and I will call upon the name of the Lord.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 I will repay my vows to the Lord, in the sight of all his people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the sight of the Lord is the death of his holy ones.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 O Lord, because I am your servant, your servant and the son of your handmaid, you have broken my bonds.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will sacrifice to you the sacrifice of praise, and I will invoke the name of the Lord.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will repay my vows to the Lord in the sight of all his people,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 in the courts of the house of the Lord, in your midst, O Jerusalem.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >